Add parallel Print Page Options

Ku Nyumba ya Wowumba Mbiya

18 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.” Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero. Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.

Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya. Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga, ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira. Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu. 10 Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.

11 “Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’ 12 Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’ ”

13 Yehova akuti,

“Uwafunse anthu a mitundu ina kuti:
    Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi?
Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita
    chinthu choopsa kwambiri.
14 Kodi chisanu chimatha pa matanthwe
    otsetsereka a phiri la Lebanoni?
Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera
    ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
15 Komatu anthu anga andiyiwala;
    akufukiza lubani kwa mafano achabechabe.
Amapunthwa mʼnjira
    zawo zakale.
Amayenda mʼnjira zachidule
    ndi kusiya njira zabwino.
16 Dziko lawo amalisandutsa chipululu,
    chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse;
onse odutsapo adzadabwa kwambiri
    ndipo adzapukusa mitu yawo.
17 Ngati mphepo yochokera kummawa,
    ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo;
ndidzawafulatira osawathandiza
    pa tsiku la mavuto awo.”

18 Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”

19 Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni;
    imvani zimene adani anga akunena za ine!
20 Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino?
    Komabe iwo andikumbira dzenje.
Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu
    kudzawapempherera
    kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
21 Choncho langani ana awo ndi njala;
    aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga.
Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye;
    amuna awo aphedwe ndi mliri,
    anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
22 Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo
    mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe.
Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo
    ndipo atchera msampha mapazi anga.
23 Koma Inu Yehova, mukudziwa
    ziwembu zawo zonse zofuna kundipha.
Musawakhululukire zolakwa zawo
    kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu.
Agonjetsedwe pamaso panu;
    muwalange muli wokwiya.”

At the Potter’s House

18 This is the word that came to Jeremiah from the Lord: “Go down to the potter’s house, and there I will give you my message.” So I went down to the potter’s house, and I saw him working at the wheel. But the pot he was shaping from the clay was marred in his hands; so the potter formed it into another pot, shaping it as seemed best to him.

Then the word of the Lord came to me. He said, “Can I not do with you, Israel, as this potter does?” declares the Lord. “Like clay(A) in the hand of the potter, so are you in my hand,(B) Israel. If at any time I announce that a nation or kingdom is to be uprooted,(C) torn down and destroyed, and if that nation I warned repents of its evil, then I will relent(D) and not inflict on it the disaster(E) I had planned. And if at another time I announce that a nation or kingdom is to be built(F) up and planted, 10 and if it does evil(G) in my sight and does not obey me, then I will reconsider(H) the good I had intended to do for it.(I)

11 “Now therefore say to the people of Judah and those living in Jerusalem, ‘This is what the Lord says: Look! I am preparing a disaster(J) for you and devising a plan(K) against you. So turn(L) from your evil ways,(M) each one of you, and reform your ways and your actions.’(N) 12 But they will reply, ‘It’s no use.(O) We will continue with our own plans; we will all follow the stubbornness of our evil hearts.(P)’”

13 Therefore this is what the Lord says:

“Inquire among the nations:
    Who has ever heard anything like this?(Q)
A most horrible(R) thing has been done
    by Virgin(S) Israel.
14 Does the snow of Lebanon
    ever vanish from its rocky slopes?
Do its cool waters from distant sources
    ever stop flowing?[a]
15 Yet my people have forgotten(T) me;
    they burn incense(U) to worthless idols,(V)
which made them stumble(W) in their ways,
    in the ancient paths.(X)
They made them walk in byways,
    on roads not built up.(Y)
16 Their land will be an object of horror(Z)
    and of lasting scorn;(AA)
all who pass by will be appalled(AB)
    and will shake their heads.(AC)
17 Like a wind(AD) from the east,
    I will scatter them before their enemies;
I will show them my back and not my face(AE)
    in the day of their disaster.”

18 They said, “Come, let’s make plans(AF) against Jeremiah; for the teaching of the law by the priest(AG) will not cease, nor will counsel from the wise,(AH) nor the word from the prophets.(AI) So come, let’s attack him with our tongues(AJ) and pay no attention to anything he says.”

19 Listen to me, Lord;
    hear what my accusers(AK) are saying!
20 Should good be repaid with evil?(AL)
    Yet they have dug a pit(AM) for me.
Remember that I stood(AN) before you
    and spoke in their behalf(AO)
    to turn your wrath away from them.
21 So give their children over to famine;(AP)
    hand them over to the power of the sword.(AQ)
Let their wives be made childless and widows;(AR)
    let their men be put to death,
    their young men(AS) slain by the sword in battle.
22 Let a cry(AT) be heard from their houses
    when you suddenly bring invaders against them,
for they have dug a pit(AU) to capture me
    and have hidden snares(AV) for my feet.
23 But you, Lord, know
    all their plots to kill(AW) me.
Do not forgive(AX) their crimes
    or blot out their sins from your sight.
Let them be overthrown before you;
    deal with them in the time of your anger.(AY)

Footnotes

  1. Jeremiah 18:14 The meaning of the Hebrew for this sentence is uncertain.