Add parallel Print Page Options

Tsiku la Masautso

16 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno, adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”

Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.” Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo. Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.

“Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo. Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’

10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’ 11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa. 12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine. 13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’ ”

14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’ 15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”

16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe. 17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa. 18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”

19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa,
    pothawirapo panga nthawi ya masautso,
anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu
    kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti,
“Makolo anthu anali ndi milungu yonama,
    anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu?
    Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”

21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa,
    kokha kano kuti adziwe
    za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga.
Pamenepo adzadziwa kuti
    dzina langa ndi Yehova.

Day of Disaster

16 Then the word of the Lord came to me: “You must not marry(A) and have sons or daughters in this place.” For this is what the Lord says about the sons and daughters born in this land and about the women who are their mothers and the men who are their fathers:(B) “They will die of deadly diseases. They will not be mourned or buried(C) but will be like dung lying on the ground.(D) They will perish by sword and famine,(E) and their dead bodies will become food for the birds and the wild animals.”(F)

For this is what the Lord says: “Do not enter a house where there is a funeral meal; do not go to mourn or show sympathy, because I have withdrawn my blessing, my love and my pity(G) from this people,” declares the Lord. “Both high and low will die in this land.(H) They will not be buried or mourned,(I) and no one will cut(J) themselves or shave(K) their head for the dead. No one will offer food(L) to comfort those who mourn(M) for the dead—not even for a father or a mother—nor will anyone give them a drink to console(N) them.

“And do not enter a house where there is feasting and sit down to eat and drink.(O) For this is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: Before your eyes and in your days I will bring an end to the sounds(P) of joy and gladness and to the voices of bride(Q) and bridegroom in this place.(R)

10 “When you tell these people all this and they ask you, ‘Why has the Lord decreed such a great disaster against us? What wrong have we done? What sin have we committed against the Lord our God?’(S) 11 then say to them, ‘It is because your ancestors forsook me,’ declares the Lord, ‘and followed other gods and served and worshiped(T) them. They forsook me and did not keep my law.(U) 12 But you have behaved more wickedly than your ancestors.(V) See how all of you are following the stubbornness of your evil hearts(W) instead of obeying me. 13 So I will throw you out of this land(X) into a land neither you nor your ancestors have known,(Y) and there you will serve other gods(Z) day and night, for I will show you no favor.’(AA)

14 “However, the days are coming,”(AB) declares the Lord, “when it will no longer be said, ‘As surely as the Lord lives, who brought the Israelites up out of Egypt,’(AC) 15 but it will be said, ‘As surely as the Lord lives, who brought the Israelites up out of the land of the north(AD) and out of all the countries where he had banished them.’(AE) For I will restore(AF) them to the land I gave their ancestors.(AG)

16 “But now I will send for many fishermen,” declares the Lord, “and they will catch them.(AH) After that I will send for many hunters, and they will hunt(AI) them down on every mountain and hill and from the crevices of the rocks.(AJ) 17 My eyes are on all their ways; they are not hidden(AK) from me, nor is their sin concealed from my eyes.(AL) 18 I will repay(AM) them double(AN) for their wickedness and their sin, because they have defiled my land(AO) with the lifeless forms of their vile images(AP) and have filled my inheritance with their detestable idols.(AQ)(AR)

19 Lord, my strength and my fortress,
    my refuge(AS) in time of distress,
to you the nations will come(AT)
    from the ends of the earth and say,
“Our ancestors possessed nothing but false gods,(AU)
    worthless idols(AV) that did them no good.(AW)
20 Do people make their own gods?
    Yes, but they are not gods!”(AX)

21 “Therefore I will teach them—
    this time I will teach them
    my power and might.
Then they will know
    that my name(AY) is the Lord.