Add parallel Print Page Options

15 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,

“ ‘Oyenera kufa adzafa;
oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;
oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;
oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’

“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.

“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?
    Kodi adzakulira ndani?
    Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.
    “Inu mukubwererabe mʼmbuyo.
Choncho Ine ndidzakukanthani.
    Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo
    monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.
Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga
    chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye
    kupambana mchenga wa kunyanja.
Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna
    dzuwa lili pamutu.
Mwadzidzidzi ndinawagwetsera
    kuwawa mtima ndi mantha.
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka
    ndipo akupuma wefuwefu.
Dzuwa lake lalowa ukanali usana;
    anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.
Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo
    kuti awaphe ndi lupanga,”
            akutero Yehova.

10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,
    munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!
Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,
    komatu aliyense akunditemberera.

11 Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.
    Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka
    ndi ya mavuto awo.

12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,
    makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Anthu ako ndi chuma chako
    ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,
chifukwa cha machimo anu onse
    a mʼdziko lanu lonse.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu
    mʼdziko limene inu simulidziwa,
chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto
    umene udzakutenthani.”

15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;
    kumbukireni ndi kundisamalira.
    Ndilipsireni anthu ondizunza.
Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.
    Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.
    Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.
Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
    ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,
    sindinasangalale nawo anthu amenewo.
Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine
    ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?
    Bwanji chilonda changa sichikupola?
Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,
    kapena ngati kasupe wopanda madzi?”

19 Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso
    ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.
Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,
    udzakhalanso mneneri wanga.
Anthu adzabwera kwa iwe
    ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba
    ngati mkuwa kwa anthu awa.
Adzalimbana nawe
    koma sadzakugonjetsa,
pakuti Ine ndili nawe
    kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”
            akutero Yehova.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
    ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

15 Then the Lord said to me: “Even if Moses(A) and Samuel(B) were to stand before me, my heart would not go out to this people.(C) Send them away from my presence!(D) Let them go! And if they ask you, ‘Where shall we go?’ tell them, ‘This is what the Lord says:

“‘Those destined for death, to death;
those for the sword, to the sword;(E)
those for starvation, to starvation;(F)
those for captivity, to captivity.’(G)

“I will send four kinds of destroyers(H) against them,” declares the Lord, “the sword(I) to kill and the dogs(J) to drag away and the birds(K) and the wild animals to devour and destroy.(L) I will make them abhorrent(M) to all the kingdoms of the earth(N) because of what Manasseh(O) son of Hezekiah king of Judah did in Jerusalem.

“Who will have pity(P) on you, Jerusalem?
    Who will mourn for you?
    Who will stop to ask how you are?
You have rejected(Q) me,” declares the Lord.
    “You keep on backsliding.
So I will reach out(R) and destroy you;
    I am tired of holding back.(S)
I will winnow(T) them with a winnowing fork
    at the city gates of the land.
I will bring bereavement(U) and destruction on my people,(V)
    for they have not changed their ways.(W)
I will make their widows(X) more numerous
    than the sand of the sea.
At midday I will bring a destroyer(Y)
    against the mothers of their young men;
suddenly I will bring down on them
    anguish and terror.(Z)
The mother of seven will grow faint(AA)
    and breathe her last.(AB)
Her sun will set while it is still day;
    she will be disgraced(AC) and humiliated.
I will put the survivors to the sword(AD)
    before their enemies,”(AE)
declares the Lord.

10 Alas, my mother, that you gave me birth,(AF)
    a man with whom the whole land strives and contends!(AG)
I have neither lent(AH) nor borrowed,
    yet everyone curses(AI) me.

11 The Lord said,

“Surely I will deliver you(AJ) for a good purpose;
    surely I will make your enemies plead(AK) with you
    in times of disaster and times of distress.

12 “Can a man break iron—
    iron from the north(AL)—or bronze?

13 “Your wealth(AM) and your treasures
    I will give as plunder,(AN) without charge,(AO)
because of all your sins
    throughout your country.(AP)
14 I will enslave you to your enemies
    in[a] a land you do not know,(AQ)
for my anger will kindle a fire(AR)
    that will burn against you.”

15 Lord, you understand;
    remember me and care for me.
    Avenge me on my persecutors.(AS)
You are long-suffering(AT)—do not take me away;
    think of how I suffer reproach for your sake.(AU)
16 When your words came, I ate(AV) them;
    they were my joy and my heart’s delight,(AW)
for I bear your name,(AX)
    Lord God Almighty.
17 I never sat(AY) in the company of revelers,
    never made merry with them;
I sat alone because your hand(AZ) was on me
    and you had filled me with indignation.
18 Why is my pain unending
    and my wound grievous and incurable?(BA)
You are to me like a deceptive brook,
    like a spring that fails.(BB)

19 Therefore this is what the Lord says:

“If you repent, I will restore you
    that you may serve(BC) me;
if you utter worthy, not worthless, words,
    you will be my spokesman.(BD)
Let this people turn to you,
    but you must not turn to them.
20 I will make you a wall(BE) to this people,
    a fortified wall of bronze;
they will fight against you
    but will not overcome(BF) you,
for I am with you
    to rescue and save you,”(BG)
declares the Lord.
21 “I will save(BH) you from the hands of the wicked(BI)
    and deliver(BJ) you from the grasp of the cruel.”(BK)

Footnotes

  1. Jeremiah 15:14 Some Hebrew manuscripts, Septuagint and Syriac (see also 17:4); most Hebrew manuscripts I will cause your enemies to bring you / into