Add parallel Print Page Options

Chilala, Njala, Lupanga

14 Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:

“Yuda akulira,
    mizinda yake ikuvutika;
anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni,
    kulira kwa Yerusalemu kwakula.
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi.
    Apita ku zitsime
    osapezako madzi.
Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi.
    Amanyazi ndi othedwa nzeru
    adziphimba kumaso.
Popeza pansi pawumiratu
    chifukwa kulibe madzi,
alimi ali ndi manyazi
    ndipo amphimba nkhope zawo.
Ngakhale mbawala yayikazi
    ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo
    chifukwa kulibe msipu.
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu
    nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe;
maso awo achita chidima
    chifukwa chosowa msipu.”

Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa,
    koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu.
Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu;
    ife takuchimwirani.
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani
    ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso,
chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno?
    Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa,
    kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa?
Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu,
    ndipo tikudziwika ndi dzina lanu;
    musatitaye ife!”

10 Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi:

“Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri;
    samatha kudziretsa.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire,
    ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo
    ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”

11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. 12 Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”

13 Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”

14 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo. 15 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala. 16 Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.

17 “Awuze mawu awa:

“ ‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza
    usana ndi usiku;
chifukwa anthu anga okondedwa
    apwetekeka kwambiri,
    akanthidwa kwambiri.
18 Ndikapita kuthengo,
    ndikuona amene aphedwa ndi lupanga;
ndikapita mu mzinda,
    ndikuona amene asakazidwa ndi njala.
Ngakhale aneneri pamodzi
    ndi ansembe onse atengedwa.’ ”

19 Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu?
    Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni?
Chifukwa chiyani mwatikantha chotere
    kuti sitingathenso kuchira?
Ife tinayembekezera mtendere
    koma palibe chabwino chomwe chabwera,
tinayembekezera kuchira
    koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu
    ndiponso kulakwa kwa makolo athu;
    ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe;
    musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero.
Kumbukirani pangano lanu ndi ife
    ndipo musachiphwanye.
22 Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina,
    kodi pali mulungu amene angagwetse mvula?
Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu,
    popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu
    amene mukhoza kuchita zimenezi.

Drought, Famine, Sword

14 This is the word of the Lord that came to Jeremiah concerning the drought:(A)

“Judah mourns,(B)
    her cities languish;
they wail for the land,
    and a cry goes up from Jerusalem.
The nobles send their servants for water;
    they go to the cisterns
    but find no water.(C)
They return with their jars unfilled;
    dismayed and despairing,
    they cover their heads.(D)
The ground is cracked
    because there is no rain in the land;(E)
the farmers are dismayed
    and cover their heads.
Even the doe in the field
    deserts her newborn fawn
    because there is no grass.(F)
Wild donkeys stand on the barren heights(G)
    and pant like jackals;
their eyes fail
    for lack of food.”(H)

Although our sins testify(I) against us,
    do something, Lord, for the sake of your name.(J)
For we have often rebelled;(K)
    we have sinned(L) against you.
You who are the hope(M) of Israel,
    its Savior(N) in times of distress,(O)
why are you like a stranger in the land,
    like a traveler who stays only a night?
Why are you like a man taken by surprise,
    like a warrior powerless to save?(P)
You are among(Q) us, Lord,
    and we bear your name;(R)
    do not forsake(S) us!

10 This is what the Lord says about this people:

“They greatly love to wander;
    they do not restrain their feet.(T)
So the Lord does not accept(U) them;
    he will now remember(V) their wickedness
    and punish them for their sins.”(W)

11 Then the Lord said to me, “Do not pray(X) for the well-being of this people. 12 Although they fast, I will not listen to their cry;(Y) though they offer burnt offerings(Z) and grain offerings,(AA) I will not accept(AB) them. Instead, I will destroy them with the sword,(AC) famine(AD) and plague.”(AE)

13 But I said, “Alas, Sovereign Lord! The prophets(AF) keep telling them, ‘You will not see the sword or suffer famine.(AG) Indeed, I will give you lasting peace(AH) in this place.’”

14 Then the Lord said to me, “The prophets are prophesying lies(AI) in my name. I have not sent(AJ) them or appointed them or spoken to them. They are prophesying to you false visions,(AK) divinations,(AL) idolatries[a] and the delusions of their own minds. 15 Therefore this is what the Lord says about the prophets who are prophesying in my name: I did not send them, yet they are saying, ‘No sword or famine will touch this land.’ Those same prophets will perish(AM) by sword and famine.(AN) 16 And the people they are prophesying to will be thrown out into the streets of Jerusalem because of the famine and sword. There will be no one to bury(AO) them, their wives, their sons and their daughters.(AP) I will pour out on them the calamity they deserve.(AQ)

17 “Speak this word to them:

“‘Let my eyes overflow with tears(AR)
    night and day without ceasing;
for the Virgin(AS) Daughter, my people,
    has suffered a grievous wound,
    a crushing blow.(AT)
18 If I go into the country,
    I see those slain by the sword;
if I go into the city,
    I see the ravages of famine.(AU)
Both prophet and priest
    have gone to a land they know not.(AV)’”

19 Have you rejected Judah completely?(AW)
    Do you despise Zion?
Why have you afflicted us
    so that we cannot be healed?(AX)
We hoped for peace
    but no good has come,
for a time of healing
    but there is only terror.(AY)
20 We acknowledge(AZ) our wickedness, Lord,
    and the guilt of our ancestors;(BA)
    we have indeed sinned(BB) against you.
21 For the sake of your name(BC) do not despise us;
    do not dishonor your glorious throne.(BD)
Remember your covenant(BE) with us
    and do not break it.
22 Do any of the worthless idols(BF) of the nations bring rain?(BG)
    Do the skies themselves send down showers?
No, it is you, Lord our God.
    Therefore our hope is in you,
    for you are the one who does all this.(BH)

Footnotes

  1. Jeremiah 14:14 Or visions, worthless divinations