Add parallel Print Page Options

Madandawulo a Yeremiya

12 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse
    ndikati nditsutsane nanu.
Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga.
    Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino?
    Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
Inu munawadzala ndipo anamera mizu;
    amakula ndi kubereka zipatso.
Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse,
    koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa;
    mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga.
Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa!
    Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti
    ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti?
Nyama ndi mbalame kulibiretu
    chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa.
Iwo amati:
    “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”

Yankho la Mulungu

Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu
    nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo?
    Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino,
udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango
    za ku Yorodani?
Ngakhale abale ako
    ndi anansi akuwukira,
    onsewo amvana zokuyimba mlandu.
Usawakhulupirire,
    ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.

“Ine ndawasiya anthu anga;
    anthu amene ndinawasankha ndawataya.
Ndapereka okondedwa anga
    mʼmanja mwa adani awo.
Anthu amene ndinawasankha
    asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango.
Akundibangulira mwaukali;
    nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
Anthu anga amene ndinawasankha
    asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga
    imene akabawi ayizinga.
Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo.
    Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa,
    anapondereza munda wanga;
munda wanga wabwino uja
    anawusandutsa chipululu.
11 Unawusandutsadi chipululu.
    Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine.
Dziko lonse lasanduka chipululu
    chifukwa palibe wolisamalira.
12 Anthu onse owononga abalalikira
    ku zitunda zonse za mʼchipululu.
Yehova watuma ankhondo ake
    kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko,
    ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga;
    anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse.
Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu
    chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”

14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo. 15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake. 16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga. 17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

Jeremiah’s Complaint

12 You are always righteous,(A) Lord,
    when I bring a case(B) before you.
Yet I would speak with you about your justice:(C)
    Why does the way of the wicked prosper?(D)
    Why do all the faithless live at ease?
You have planted(E) them, and they have taken root;
    they grow and bear fruit.(F)
You are always on their lips
    but far from their hearts.(G)
Yet you know me, Lord;
    you see me and test(H) my thoughts about you.
Drag them off like sheep(I) to be butchered!
    Set them apart for the day of slaughter!(J)
How long will the land lie parched(K)
    and the grass in every field be withered?(L)
Because those who live in it are wicked,
    the animals and birds have perished.(M)
Moreover, the people are saying,
    “He will not see what happens to us.”

God’s Answer

“If you have raced with men on foot
    and they have worn you out,
    how can you compete with horses?
If you stumble[a] in safe country,
    how will you manage in the thickets(N) by[b] the Jordan?
Your relatives, members of your own family—
    even they have betrayed you;
    they have raised a loud cry against you.(O)
Do not trust them,
    though they speak well of you.(P)

“I will forsake(Q) my house,
    abandon(R) my inheritance;
I will give the one I love(S)
    into the hands of her enemies.(T)
My inheritance has become to me
    like a lion(U) in the forest.
She roars at me;
    therefore I hate her.(V)
Has not my inheritance become to me
    like a speckled bird of prey
    that other birds of prey surround and attack?
Go and gather all the wild beasts;
    bring them to devour.(W)
10 Many shepherds(X) will ruin my vineyard
    and trample down my field;
they will turn my pleasant field
    into a desolate wasteland.(Y)
11 It will be made a wasteland,(Z)
    parched and desolate before me;(AA)
the whole land will be laid waste
    because there is no one who cares.
12 Over all the barren heights in the desert
    destroyers will swarm,
for the sword(AB) of the Lord(AC) will devour(AD)
    from one end of the land to the other;(AE)
    no one will be safe.(AF)
13 They will sow wheat but reap thorns;
    they will wear themselves out but gain nothing.(AG)
They will bear the shame of their harvest
    because of the Lord’s fierce anger.”(AH)

14 This is what the Lord says: “As for all my wicked neighbors who seize the inheritance(AI) I gave my people Israel, I will uproot(AJ) them from their lands and I will uproot(AK) the people of Judah from among them. 15 But after I uproot them, I will again have compassion(AL) and will bring(AM) each of them back to their own inheritance and their own country. 16 And if they learn(AN) well the ways of my people and swear by my name, saying, ‘As surely as the Lord lives’(AO)—even as they once taught my people to swear by Baal(AP)—then they will be established among my people.(AQ) 17 But if any nation does not listen, I will completely uproot and destroy(AR) it,” declares the Lord.

Footnotes

  1. Jeremiah 12:5 Or you feel secure only
  2. Jeremiah 12:5 Or the flooding of