Add parallel Print Page Options

Rute ndi Bowazi ku Malo Wopunthira Tirigu ndi Barele

Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino? Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira. Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa. Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”

Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”

Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.

Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.

Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.

Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”

10 Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka. 11 Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino. 12 Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine. 13 Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”

14 Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”

15 Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.

16 Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.

17 Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”

18 Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

Ruth and Boaz at the Threshing Floor

One day Ruth’s mother-in-law Naomi(A) said to her, “My daughter, I must find a home[a](B) for you, where you will be well provided for. Now Boaz, with whose women you have worked, is a relative(C) of ours. Tonight he will be winnowing barley on the threshing floor.(D) Wash,(E) put on perfume,(F) and get dressed in your best clothes.(G) Then go down to the threshing floor, but don’t let him know you are there until he has finished eating and drinking.(H) When he lies down, note the place where he is lying. Then go and uncover his feet and lie down. He will tell you what to do.”

“I will do whatever you say,”(I) Ruth answered. So she went down to the threshing floor(J) and did everything her mother-in-law told her to do.

When Boaz had finished eating and drinking and was in good spirits,(K) he went over to lie down at the far end of the grain pile.(L) Ruth approached quietly, uncovered his feet and lay down. In the middle of the night something startled the man; he turned—and there was a woman lying at his feet!

“Who are you?” he asked.

“I am your servant Ruth,” she said. “Spread the corner of your garment(M) over me, since you are a guardian-redeemer[b](N) of our family.”

10 “The Lord bless you,(O) my daughter,” he replied. “This kindness is greater than that which you showed earlier:(P) You have not run after the younger men, whether rich or poor. 11 And now, my daughter, don’t be afraid. I will do for you all you ask. All the people of my town know that you are a woman of noble character.(Q) 12 Although it is true that I am a guardian-redeemer of our family,(R) there is another who is more closely related than(S) I. 13 Stay here for the night, and in the morning if he wants to do his duty as your guardian-redeemer,(T) good; let him redeem you. But if he is not willing, as surely as the Lord lives(U) I will do it.(V) Lie here until morning.”

14 So she lay at his feet until morning, but got up before anyone could be recognized; and he said, “No one must know that a woman came to the threshing floor.(W)(X)

15 He also said, “Bring me the shawl(Y) you are wearing and hold it out.” When she did so, he poured into it six measures of barley and placed the bundle on her. Then he[c] went back to town.

16 When Ruth came to her mother-in-law, Naomi asked, “How did it go, my daughter?”

Then she told her everything Boaz had done for her 17 and added, “He gave me these six measures of barley, saying, ‘Don’t go back to your mother-in-law empty-handed.’”

18 Then Naomi said, “Wait, my daughter, until you find out what happens. For the man will not rest until the matter is settled today.”(Z)

Footnotes

  1. Ruth 3:1 Hebrew find rest (see 1:9)
  2. Ruth 3:9 The Hebrew word for guardian-redeemer is a legal term for one who has the obligation to redeem a relative in serious difficulty (see Lev. 25:25-55); also in verses 12 and 13.
  3. Ruth 3:15 Most Hebrew manuscripts; many Hebrew manuscripts, Vulgate and Syriac she