Add parallel Print Page Options

Nyimbo ya Debora

“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;
    ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,
    tamandani Yehova:

“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!
    Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,
    Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,
    pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,
dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka
    nigwetsa madzi.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,
    Mulungu wa Israeli.

“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,
    pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;
    alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi
    mpaka pamene iwe Debora unafika;
    unafika ngati mayi ku Israeli.
Pamene anasankha milungu ina,
    nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,
ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke
    pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,
    uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.
    Tamandani Yehova!

10 “Inu okwera pa abulu oyera,
    okhala pa zishalo,
    ndi inu oyenda pa msewu,
yankhulani. 11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;
    kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;
    akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova
    anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;
    tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.
Iwe Baraki! nyamuka
    Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13 “Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;
    anthu a Yehova anapita
kukamenyera Yehova nkhondo
    kulimbana ndi adani amphamvu.
14 Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;
    akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.
Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,
    ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
15 Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;
    inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,
    ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.
Koma pakati pa mafuko a Rubeni
    panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
16 Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera
    zitoliro zoyitanira nkhosa?
Pakati pa anthu a fuko la Rubeni
    panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
17 Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.
    Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?
Aseri anali pa gombe la Nyanja;
    anangokhala mʼmadooko mwawo.
18 Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.
    Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19 “Mafumu anabwera, anachita nkhondo;
    mafumu Akanaani anachita nkhondo
ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,
    koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
20 Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,
    zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,
    chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.
    Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
22 Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,
    akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
23 Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’
    ‘Tembererani nzika zake mwaukali,
chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,
    kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24 “Akhale wodala kupambana akazi onse,
    Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;
    inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
25 Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;
    anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
26 Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,
    anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.
Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,
    ndi kumubowola mu litsipa mwake.
27 Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,
    anagwa; iye anagona pamenepo.
Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;
    pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28 “Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;
    nafuwula mokweza kuti,
‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?
    Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
29 Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,
    ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
30 ‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;
    akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.
    Sisera akumupatsa zofunkha:
    zovala zonyikidwa mu utoto,
    zoti ndizivala mʼkhosi
zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31 “Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,
    koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa
    pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

The Song of Deborah

On that day Deborah(A) and Barak son of Abinoam(B) sang this song:(C)

“When the princes in Israel take the lead,
    when the people willingly offer(D) themselves—
    praise the Lord!(E)

“Hear this, you kings! Listen, you rulers!
    I, even I, will sing to[a] the Lord;(F)
    I will praise the Lord, the God of Israel, in song.(G)

“When you, Lord, went out(H) from Seir,(I)
    when you marched from the land of Edom,
the earth shook,(J) the heavens poured,
    the clouds poured down water.(K)
The mountains quaked(L) before the Lord, the One of Sinai,
    before the Lord, the God of Israel.

“In the days of Shamgar son of Anath,(M)
    in the days of Jael,(N) the highways(O) were abandoned;
    travelers took to winding paths.(P)
Villagers in Israel would not fight;
    they held back until I, Deborah,(Q) arose,
    until I arose, a mother in Israel.
God chose new leaders(R)
    when war came to the city gates,(S)
but not a shield or spear(T) was seen
    among forty thousand in Israel.
My heart is with Israel’s princes,
    with the willing volunteers(U) among the people.
    Praise the Lord!

10 “You who ride on white donkeys,(V)
    sitting on your saddle blankets,
    and you who walk along the road,
consider 11 the voice of the singers[b] at the watering places.
    They recite the victories(W) of the Lord,
    the victories of his villagers in Israel.

“Then the people of the Lord
    went down to the city gates.(X)
12 ‘Wake up,(Y) wake up, Deborah!(Z)
    Wake up, wake up, break out in song!
Arise, Barak!(AA)
    Take captive your captives,(AB) son of Abinoam.’

13 “The remnant of the nobles came down;
    the people of the Lord came down to me against the mighty.
14 Some came from Ephraim,(AC) whose roots were in Amalek;(AD)
    Benjamin(AE) was with the people who followed you.
From Makir(AF) captains came down,
    from Zebulun those who bear a commander’s[c] staff.
15 The princes of Issachar(AG) were with Deborah;(AH)
    yes, Issachar was with Barak,(AI)
    sent under his command into the valley.
In the districts of Reuben
    there was much searching of heart.
16 Why did you stay among the sheep pens[d](AJ)
    to hear the whistling for the flocks?(AK)
In the districts of Reuben
    there was much searching of heart.
17 Gilead(AL) stayed beyond the Jordan.
    And Dan, why did he linger by the ships?
Asher(AM) remained on the coast(AN)
    and stayed in his coves.
18 The people of Zebulun(AO) risked their very lives;
    so did Naphtali(AP) on the terraced fields.(AQ)

19 “Kings came(AR), they fought,
    the kings of Canaan fought.
At Taanach, by the waters of Megiddo,(AS)
    they took no plunder of silver.(AT)
20 From the heavens(AU) the stars fought,
    from their courses they fought against Sisera.
21 The river Kishon(AV) swept them away,
    the age-old river, the river Kishon.
    March on, my soul; be strong!(AW)
22 Then thundered the horses’ hooves—
    galloping, galloping go his mighty steeds.(AX)
23 ‘Curse Meroz,’ said the angel of the Lord.
    ‘Curse its people bitterly,
because they did not come to help the Lord,
    to help the Lord against the mighty.’

24 “Most blessed of women(AY) be Jael,(AZ)
    the wife of Heber the Kenite,(BA)
    most blessed of tent-dwelling women.
25 He asked for water, and she gave him milk;(BB)
    in a bowl fit for nobles she brought him curdled milk.
26 Her hand reached for the tent peg,
    her right hand for the workman’s hammer.
She struck Sisera, she crushed his head,
    she shattered and pierced his temple.(BC)
27 At her feet he sank,
    he fell; there he lay.
At her feet he sank, he fell;
    where he sank, there he fell—dead(BD).

28 “Through the window(BE) peered Sisera’s mother;
    behind the lattice she cried out,(BF)
‘Why is his chariot so long in coming?
    Why is the clatter of his chariots delayed?’
29 The wisest of her ladies answer her;
    indeed, she keeps saying to herself,
30 ‘Are they not finding and dividing the spoils:(BG)
    a woman or two for each man,
colorful garments as plunder for Sisera,
    colorful garments embroidered,
highly embroidered garments(BH) for my neck—
    all this as plunder?(BI)

31 “So may all your enemies perish,(BJ) Lord!
    But may all who love you be like the sun(BK)
    when it rises in its strength.”(BL)

Then the land had peace(BM) forty years.

Footnotes

  1. Judges 5:3 Or of
  2. Judges 5:11 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  3. Judges 5:14 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  4. Judges 5:16 Or the campfires; or the saddlebags