Add parallel Print Page Options

Debora

Ehudi atamwalira, Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova. Choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Yabini, mfumu ya ku Kanaani, imene inkalamulira ku Hazori. Mkulu wa ankhondo ake anali Sisera, amene ankakhala ku Haroseti-Hagoyimu. Aisraeli analira kwa Yehova kuti awathandize, chifukwa Sisera anali ndi magaleta achitsulo 900 ndipo anazunza Aisraeli mwankhanza kwa zaka makumi awiri.

Debora, mneneri wamkazi, mkazi wake wa Rapidoti ndiye ankatsogolera Israeli nthawi imeneyo. Iye ankakhala pansi pa mtengo wa mgwalangwa wa Debora, pakati pa Rama ndi Beteli mʼdziko la ku mapiri la Efereimu, ndipo Aisraeli ankapita kwa iye kuti akaweruze milandu yawo. Debora uja anatuma munthu kuti akayitane Baraki mwana wa Abinoamu wa ku Kedesi mʼdziko la Nafutali ndipo anati kwa iye, “Yehova Mulungu wa Israeli akukulamula iwe kuti, ‘Pita kasonkhanitse anthu ku phiri la Tabori. Ubwere nawo anthu 10,000 a fuko la Nafutali ndi a fuko la Zebuloni. Ine ndidzakokera Sisera mkulu wa ankhondo a Yabini pamodzi ndi magaleta ake ndi asilikali ake kwa inu ku mtsinje wa Kisoni ndipo ndidzamupereka mʼmanja mwanu.’ ”

Baraki anamuyankha kuti, “Mukapita nane limodzi ine ndipita. Koma ngati sitipitira limodzi, inenso sindipita.”

Debora anati, “Chabwino, ine ndipita nawe limodzi. Koma mudziwe kuti inu simudzalandirapo ulemu pa zimene mwachitazi popeza Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwa munthu wamkazi.” Choncho Debora ananyamuka kupita ku Kedesi pamodzi ndi Baraki. 10 Baraki anayitana mafuko a Zebuloni ndi Nafutali kuti abwere ku Kedesi. Anthu 10,000 anamutsatira, ndipo Debora anapita naye pamodzi.

11 Nthawi imeneyo nʼkuti Mkeni wina dzina lake Heberi atalekana ndi Akeni anzake, zidzukulu za Hobabu, mlamu wa Mose, nakamanga tenti yake pafupi ndi mtengo wa thundu ku Zananimu pafupi ndi Kedesi.

12 Pamene Sisera anamva kuti Baraki mwana wa Abinoamu wapita ku phiri la Tabori, 13 anasonkhanitsa magaleta ake achitsulo 900 ndi anthu onse amene anali naye ndipo anachoka ku Haroseti-Hagoyimu kupita ku mtsinje wa Kisoni.

14 Debora anawuza Baraki kuti, “Dzukani! Paja ndi lero limene Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwako. Kodi Yehova sanakhale akukutsogolerani?” Choncho Baraki anatsika phiri la Tabori, anthu 10,000 akumutsata. 15 Yehova anasokoneza Sisera ndi magaleta ake pamodzi ndi ankhondo ake onse. Baraki ndi anthu ake anawapirikitsa ndipo Sisera anatsika pa galeta yake nayamba kuthawa pansi. 16 Baraki analondola magaletawo pamodzi ndi ankhondo onse mpaka ku Haroseti-Hagoyimu, ndipo ankhondo onse a Sisera anaphedwa ndi lupanga. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe anatsala.

17 Komabe Sisera anathawa pansi mpaka anakafika ku tenti ya Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni uja, chifukwa panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori ndi banja la Heberi, Mkeni uja.

18 Yaeli anatuluka kukachingamira Sisera ndipo anati, “Bwerani mbuye wanga, lowani momwemo musaope.” Choncho analowa mʼtenti muja, ndipo anamufunditsa chofunda.

19 Anati, “Ndili ndi ludzu, chonde patseniko madzi pangʼono akumwa, ndili ndi ludzu.” Mkaziyo anatsekula thumba la chikopa mmene munali mkaka, namupatsa kuti amwe, ndipo anamufunditsanso.

20 Kenaka anawuza mkaziyo kuti, “Muyime pa khomo la tentili, ndipo munthu wina akabwera kudzakufunsani kuti, ‘Kodi kwafika munthu wina kuno?’ Inu muyankha kuti, ‘Ayi.’ ”

21 Koma Yaeli mkazi wa Heberi, anatenga chikhomo cha tenti ndi hamara ndi kupita mwakachetechete kwa Sisera uja. Tsono Sisera ali mtulo chifukwa chotopa, mkazi uja anamukhomera chikhomo chija mʼmutu mwake. Chinatulukira kwinaku mpaka kulowa mʼnthaka, ndipo anafa pomwepo.

22 Baraki atafika akulondola Sisera, Yaeli anatuluka kukamuchingamira namuwuza kuti, “Lowani mudzaone munthu amene mukumufunafuna.” Tsono atalowa anangoona Sisera ali thapsa pansi wakufa ndi chikhomo chili mʼmutu mwake.

23 “Choncho pa tsiku limenelo Mulungu anagonjetsa Yabini mfumu ya Akanaani, pamaso pa Aisraeli. 24 Ndipo Aisraeli anapanikizabe Yabini, mfumu ya Akanaani, mpaka kumuwonongeratu.

Deborah

Again the Israelites did evil(A) in the eyes of the Lord,(B) now that Ehud(C) was dead. So the Lord sold them(D) into the hands of Jabin king of Canaan, who reigned in Hazor.(E) Sisera,(F) the commander of his army, was based in Harosheth Haggoyim. Because he had nine hundred chariots fitted with iron(G) and had cruelly oppressed(H) the Israelites for twenty years, they cried to the Lord for help.

Now Deborah,(I) a prophet,(J) the wife of Lappidoth, was leading[a] Israel at that time. She held court(K) under the Palm of Deborah between Ramah(L) and Bethel(M) in the hill country of Ephraim, and the Israelites went up to her to have their disputes decided. She sent for Barak son of Abinoam(N) from Kedesh(O) in Naphtali and said to him, “The Lord, the God of Israel, commands you: ‘Go, take with you ten thousand men of Naphtali(P) and Zebulun(Q) and lead them up to Mount Tabor.(R) I will lead Sisera, the commander of Jabin’s(S) army, with his chariots and his troops to the Kishon River(T) and give him into your hands.(U)’”

Barak said to her, “If you go with me, I will go; but if you don’t go with me, I won’t go.”

“Certainly I will go with you,” said Deborah. “But because of the course you are taking, the honor will not be yours, for the Lord will deliver Sisera into the hands of a woman.” So Deborah went with Barak to Kedesh.(V) 10 There Barak summoned(W) Zebulun and Naphtali, and ten thousand men went up under his command. Deborah also went up with him.

11 Now Heber the Kenite had left the other Kenites,(X) the descendants of Hobab,(Y) Moses’ brother-in-law,[b] and pitched his tent by the great tree(Z) in Zaanannim(AA) near Kedesh.

12 When they told Sisera that Barak son of Abinoam had gone up to Mount Tabor,(AB) 13 Sisera summoned from Harosheth Haggoyim to the Kishon River(AC) all his men and his nine hundred chariots fitted with iron.(AD)

14 Then Deborah said to Barak, “Go! This is the day the Lord has given Sisera into your hands.(AE) Has not the Lord gone ahead(AF) of you?” So Barak went down Mount Tabor, with ten thousand men following him. 15 At Barak’s advance, the Lord routed(AG) Sisera and all his chariots and army by the sword, and Sisera got down from his chariot and fled on foot.

16 Barak pursued the chariots and army as far as Harosheth Haggoyim, and all Sisera’s troops fell by the sword; not a man was left.(AH) 17 Sisera, meanwhile, fled on foot to the tent of Jael,(AI) the wife of Heber the Kenite,(AJ) because there was an alliance between Jabin king of Hazor(AK) and the family of Heber the Kenite.

18 Jael(AL) went out to meet Sisera and said to him, “Come, my lord, come right in. Don’t be afraid.” So he entered her tent, and she covered him with a blanket.

19 “I’m thirsty,” he said. “Please give me some water.” She opened a skin of milk,(AM) gave him a drink, and covered him up.

20 “Stand in the doorway of the tent,” he told her. “If someone comes by and asks you, ‘Is anyone in there?’ say ‘No.’”

21 But Jael,(AN) Heber’s wife, picked up a tent peg and a hammer and went quietly to him while he lay fast asleep,(AO) exhausted. She drove the peg through his temple into the ground, and he died.(AP)

22 Just then Barak came by in pursuit of Sisera, and Jael(AQ) went out to meet him. “Come,” she said, “I will show you the man you’re looking for.” So he went in with her, and there lay Sisera with the tent peg through his temple—dead.(AR)

23 On that day God subdued(AS) Jabin(AT) king of Canaan before the Israelites. 24 And the hand of the Israelites pressed harder and harder against Jabin king of Canaan until they destroyed him.(AU)

Footnotes

  1. Judges 4:4 Traditionally judging
  2. Judges 4:11 Or father-in-law