Add parallel Print Page Options

Masomphenya a Obadiya

Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:
    Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,
“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;
    udzanyozedwa kwambiri.
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
    iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe
    ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,
iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,
    ‘Ndani anganditsitse pansi?’
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga
    ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,
    ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
            akutero Yehova.
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,
    kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,
aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!
    Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Ngati anthu othyola mphesa akanafika,
    kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,
    chuma chake chobisika chidzabedwa!
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;
    abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;
amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,
    koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,
    kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,
    anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,
    ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau
    adzaphedwa pa nkhondo.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,
    udzakhala wamanyazi;
    adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Pamene adani
    ankamulanda chuma chake
pamene alendo analowa pa zipata zake
    ndi kuchita maere pa Yerusalemu,
    pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako
    pa nthawi ya tsoka lake,
kapena kunyogodola Ayuda
    chifukwa cha chiwonongeko chawo,
kapena kuwaseka pa nthawi ya
    mavuto awo.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga
    pa nthawi ya masautso awo,
kapena kuwanyogodola
    pa tsiku la tsoka lawo,
kapena kulanda chuma chawo
    pa nthawi ya masautso awo.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu
    kuti uphe Ayuda othawa,
kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka
    pa nthawi ya mavuto awo.”

15 “Tsiku la Yehova layandikira
    limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.
Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;
    zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera,
    koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;
iwo adzamwa ndi kudzandira
    ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;
    phirilo lidzakhala lopatulika,
ndipo nyumba ya Yakobo
    idzalandira cholowa chake.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto
    ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;
nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,
    ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.
Sipadzakhala anthu opulumuka
    kuchokera mʼnyumba ya Esau.”
            Yehova wayankhula.

19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala
    ku mapiri a Esau,
ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri
    adzatenga dziko la Afilisti.
Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,
    ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo
    adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;
a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi
    adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni
    ndipo adzalamulira mapiri a Esau.
    Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

Obadiah’s Vision(A)(B)

The vision(C) of Obadiah.

This is what the Sovereign Lord says about Edom(D)

We have heard a message from the Lord:
    An envoy(E) was sent to the nations to say,
“Rise, let us go against her for battle”(F)

“See, I will make you small(G) among the nations;
    you will be utterly despised.
The pride(H) of your heart has deceived you,
    you who live in the clefts of the rocks[a](I)
    and make your home on the heights,
you who say to yourself,
    ‘Who can bring me down to the ground?’(J)
Though you soar like the eagle
    and make your nest(K) among the stars,
    from there I will bring you down,”(L)
declares the Lord.(M)
“If thieves came to you,
    if robbers in the night—
oh, what a disaster awaits you!—
    would they not steal only as much as they wanted?
If grape pickers came to you,
    would they not leave a few grapes?(N)
But how Esau will be ransacked,
    his hidden treasures pillaged!
All your allies(O) will force you to the border;
    your friends will deceive and overpower you;
those who eat your bread(P) will set a trap for you,[b]
    but you will not detect it.

“In that day,” declares the Lord,
    “will I not destroy(Q) the wise men of Edom,
    those of understanding in the mountains of Esau?
Your warriors, Teman,(R) will be terrified,
    and everyone in Esau’s mountains
    will be cut down in the slaughter.
10 Because of the violence(S) against your brother Jacob,(T)
    you will be covered with shame;
    you will be destroyed forever.(U)
11 On the day you stood aloof
    while strangers carried off his wealth
and foreigners entered his gates
    and cast lots(V) for Jerusalem,
    you were like one of them.(W)
12 You should not gloat(X) over your brother
    in the day of his misfortune,(Y)
nor rejoice(Z) over the people of Judah
    in the day of their destruction,(AA)
nor boast(AB) so much
    in the day of their trouble.(AC)
13 You should not march through the gates of my people
    in the day of their disaster,
nor gloat over them in their calamity(AD)
    in the day of their disaster,
nor seize their wealth
    in the day of their disaster.
14 You should not wait at the crossroads
    to cut down their fugitives,(AE)
nor hand over their survivors
    in the day of their trouble.

15 “The day of the Lord is near(AF)
    for all nations.
As you have done, it will be done to you;
    your deeds(AG) will return upon your own head.
16 Just as you drank(AH) on my holy hill,(AI)
    so all the nations will drink(AJ) continually;
they will drink and drink
    and be as if they had never been.(AK)
17 But on Mount Zion will be deliverance;(AL)
    it will be holy,(AM)
    and Jacob will possess his inheritance.(AN)
18 Jacob will be a fire
    and Joseph a flame;
Esau will be stubble,
    and they will set him on fire(AO) and destroy(AP) him.
There will be no survivors(AQ)
    from Esau.”
The Lord has spoken.

19 People from the Negev will occupy
    the mountains of Esau,
and people from the foothills will possess
    the land of the Philistines.(AR)
They will occupy the fields of Ephraim and Samaria,(AS)
    and Benjamin(AT) will possess Gilead.
20 This company of Israelite exiles who are in Canaan
    will possess the land as far as Zarephath;(AU)
the exiles from Jerusalem who are in Sepharad
    will possess the towns of the Negev.(AV)
21 Deliverers(AW) will go up on[c] Mount Zion
    to govern the mountains of Esau.
    And the kingdom will be the Lord’s.(AX)

Footnotes

  1. Obadiah 1:3 Or of Sela
  2. Obadiah 1:7 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.
  3. Obadiah 1:21 Or from