Add parallel Print Page Options

Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola
    mu nsapato wavalazo!
Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,
    ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino
    chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.
Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu
    utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,
    ngati mphoyo zamapasa.
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.
Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,
    amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.
Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,
    yoyangʼana ku Damasiko.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.
    Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;
    mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,
    iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,
    ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;
    ndidzathyola zipatso zake.”
Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,
    fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
    ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,
    ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 Wokondedwayo ine ndine wake,
    ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,
    tikagone ku midzi.
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,
    tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,
ngati maluwa ake ayamba kuoneka,
    komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.
    Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,
    ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,
zatsopano ndi zakale zomwe,
    zimene ndakusungira wokondedwa wanga.

[a]How beautiful your sandaled feet,
    O prince’s(A) daughter!
Your graceful legs are like jewels,
    the work of an artist’s hands.
Your navel is a rounded goblet
    that never lacks blended wine.
Your waist is a mound of wheat
    encircled by lilies.
Your breasts(B) are like two fawns,
    like twin fawns of a gazelle.
Your neck is like an ivory tower.(C)
Your eyes are the pools of Heshbon(D)
    by the gate of Bath Rabbim.
Your nose is like the tower of Lebanon(E)
    looking toward Damascus.
Your head crowns you like Mount Carmel.(F)
    Your hair is like royal tapestry;
    the king is held captive by its tresses.
How beautiful(G) you are and how pleasing,
    my love, with your delights!(H)
Your stature is like that of the palm,
    and your breasts(I) like clusters of fruit.
I said, “I will climb the palm tree;
    I will take hold of its fruit.”
May your breasts be like clusters of grapes on the vine,
    the fragrance of your breath like apples,(J)
    and your mouth like the best wine.

She

May the wine go straight to my beloved,(K)
    flowing gently over lips and teeth.[b]
10 I belong to my beloved,
    and his desire(L) is for me.(M)
11 Come, my beloved, let us go to the countryside,
    let us spend the night in the villages.[c]
12 Let us go early to the vineyards(N)
    to see if the vines have budded,(O)
if their blossoms(P) have opened,
    and if the pomegranates(Q) are in bloom(R)
    there I will give you my love.
13 The mandrakes(S) send out their fragrance,
    and at our door is every delicacy,
both new and old,
    that I have stored up for you, my beloved.(T)

Footnotes

  1. Song of Songs 7:1 In Hebrew texts 7:1-13 is numbered 7:2-14.
  2. Song of Songs 7:9 Septuagint, Aquila, Vulgate and Syriac; Hebrew lips of sleepers
  3. Song of Songs 7:11 Or the henna bushes