Add parallel Print Page Options

Mwamuna

Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga!
    Ndithudi, ndiwe wokongola!
    Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
    zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene,
    zochokera kozisambitsa kumene.
Iliyonse ili ndi ana amapasa;
    palibe imene ili yokha.
Milomo yako ili ngati mbota yofiira;
    pakamwa pako ndi pokongola kwambiri.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba
    kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide,
    yomangidwa bwino ndi yosalala;
pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000,
    zishango zonsezo za anthu ankhondo.
Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala,
    ngati ana amapasa a nswala
    amene akudya pakati pa maluwa okongola.
Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira
    ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,
ndidzapita ku phiri la mure
    ndi ku chitunda cha lubani.
Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga;
    palibe chilema pa iwe.

Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga,
    tiye tichoke ku Lebanoni,
utsikepo pa msonga ya Amana,
    kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni,
kuchoka ku mapanga a mikango
    ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima,
    iwe wanditenga mtima
ndi kapenyedwe ka maso ako,
    ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa!
    Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo,
    ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi;
    pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi.
    Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa;
    ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza;
    muli zipatso zokoma kwambiri,
    muli hena ndi nadi,
14     nadi ndi safiro,
    kalamusi ndi sinamoni,
    komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino.
    Mulinso mure ndi aloe
    ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda,
    chitsime cha madzi oyenda,
    mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.

Mkazi

16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto,
    ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera!
Uzira pa munda wanga,
    kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse.
Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake
    ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

He

How beautiful you are, my darling!
    Oh, how beautiful!
    Your eyes behind your veil(A) are doves.(B)
Your hair is like a flock of goats
    descending from the hills of Gilead.(C)
Your teeth are like a flock of sheep just shorn,
    coming up from the washing.
Each has its twin;
    not one of them is alone.(D)
Your lips are like a scarlet ribbon;
    your mouth(E) is lovely.(F)
Your temples behind your veil
    are like the halves of a pomegranate.(G)
Your neck is like the tower(H) of David,
    built with courses of stone[a];
on it hang a thousand shields,(I)
    all of them shields of warriors.
Your breasts(J) are like two fawns,
    like twin fawns of a gazelle(K)
    that browse among the lilies.(L)
Until the day breaks
    and the shadows flee,(M)
I will go to the mountain of myrrh(N)
    and to the hill of incense.
You are altogether beautiful,(O) my darling;
    there is no flaw(P) in you.

Come with me from Lebanon, my bride,(Q)
    come with me from Lebanon.
Descend from the crest of Amana,
    from the top of Senir,(R) the summit of Hermon,(S)
from the lions’ dens
    and the mountain haunts of leopards.
You have stolen my heart, my sister, my bride;(T)
    you have stolen my heart
with one glance of your eyes,
    with one jewel of your necklace.(U)
10 How delightful(V) is your love(W), my sister, my bride!
    How much more pleasing is your love than wine,(X)
and the fragrance of your perfume(Y)
    more than any spice!
11 Your lips drop sweetness as the honeycomb, my bride;
    milk and honey are under your tongue.(Z)
The fragrance of your garments
    is like the fragrance of Lebanon.(AA)
12 You are a garden(AB) locked up, my sister, my bride;(AC)
    you are a spring enclosed, a sealed fountain.(AD)
13 Your plants are an orchard of pomegranates(AE)
    with choice fruits,
    with henna(AF) and nard,
14     nard and saffron,
    calamus and cinnamon,(AG)
    with every kind of incense tree,
    with myrrh(AH) and aloes(AI)
    and all the finest spices.(AJ)
15 You are[b] a garden(AK) fountain,(AL)
    a well of flowing water
    streaming down from Lebanon.

She

16 Awake, north wind,
    and come, south wind!
Blow on my garden,(AM)
    that its fragrance(AN) may spread everywhere.
Let my beloved(AO) come into his garden
    and taste its choice fruits.(AP)

Footnotes

  1. Song of Songs 4:4 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  2. Song of Songs 4:15 Or I am (spoken by She)