Nyimbo ya Solomoni 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
3 Usiku wonse ndili pa bedi langa
ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;
ndinamufunafuna koma osamupeza.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,
mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;
ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.
Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
3 Alonda anandipeza
pamene ankayendera mzinda.
“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
4 Nditawapitirira pangʼono
ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.
Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke
mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,
mʼchipinda cha amene anandibereka.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani
pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:
Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa
mpaka pamene chifunire ichocho.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu
ngati utsi watolotolo,
wonunkhira mure ndi lubani,
zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,
choperekezedwa ndi asilikali 60,
anthu amphamvu a ku Israeli,
8 onse atanyamula lupanga,
onse odziwa bwino nkhondo,
aliyense ali ndi lupanga pambali pake,
kukonzekera zoopsa za usiku.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;
anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva,
kumbuyo kwake kwa golide.
Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,
anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi
cha akazi a ku Yerusalemu.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni
ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,
chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka
pa tsiku la ukwati wake,
tsiku limene mtima wake unasangalala.
Song of Songs 3
New International Version
3 All night long on my bed
I looked(A) for the one my heart loves;
I looked for him but did not find him.
2 I will get up now and go about the city,
through its streets and squares;
I will search for the one my heart loves.
So I looked for him but did not find him.
3 The watchmen found me
as they made their rounds in the city.(B)
“Have you seen the one my heart loves?”
4 Scarcely had I passed them
when I found the one my heart loves.
I held him and would not let him go
till I had brought him to my mother’s house,(C)
to the room of the one who conceived me.(D)
5 Daughters of Jerusalem, I charge you(E)
by the gazelles and by the does of the field:
Do not arouse or awaken love
until it so desires.(F)
6 Who is this coming up from the wilderness(G)
like a column of smoke,
perfumed with myrrh(H) and incense
made from all the spices(I) of the merchant?
7 Look! It is Solomon’s carriage,
escorted by sixty warriors,(J)
the noblest of Israel,
8 all of them wearing the sword,
all experienced in battle,
each with his sword at his side,
prepared for the terrors of the night.(K)
9 King Solomon made for himself the carriage;
he made it of wood from Lebanon.
10 Its posts he made of silver,
its base of gold.
Its seat was upholstered with purple,
its interior inlaid with love.
Daughters of Jerusalem, 11 come out,
and look, you daughters of Zion.(L)
Look[a] on King Solomon wearing a crown,
the crown with which his mother crowned him
on the day of his wedding,
the day his heart rejoiced.(M)
Footnotes
- Song of Songs 3:11 Or interior lovingly inlaid / by the daughters of Jerusalem. / 11 Come out, you daughters of Zion, / and look
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.