Add parallel Print Page Options

Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Mkazi

Undipsompsone ndi milomo yako
    chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;
    dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.
    Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!
    Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.

Abwenzi

Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,
    tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.

Mkazi

Amachita bwinotu potamanda iwe!

Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,
    inu akazi a ku Yerusalemu,
    ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,
    ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,
    ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.
Alongo anga anandikwiyira
    ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;
    munda wangawanga sindinawusamalire.
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako
    ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.
Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere
    pambali pa ziweto za abwenzi ako?

Abwenzi

Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,
    ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa
ndipo udyetse ana ambuzi
    pambali pa matenti a abusa.

Mwamuna

Iwe bwenzi langa,
    uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,
    khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide
    zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.

Mkazi

12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,
    mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,
    kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,
    ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.

Mwamuna

15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!
    Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,
    maso ako ali ngati nkhunda.

Mkazi

16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!
    Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!
    Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.

Mwamuna

17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,
    phaso lake ndi la mtengo wa payini.

Solomon’s Song of Songs.(A)

She[a]

Let him kiss me with the kisses of his mouth—
    for your love(B) is more delightful than wine.(C)
Pleasing is the fragrance of your perfumes;(D)
    your name(E) is like perfume poured out.
    No wonder the young women(F) love you!
Take me away with you—let us hurry!
    Let the king bring me into his chambers.(G)

Friends

We rejoice and delight(H) in you[b];
    we will praise your love(I) more than wine.

She

How right they are to adore you!

Dark am I, yet lovely,(J)
    daughters of Jerusalem,(K)
dark like the tents of Kedar,(L)
    like the tent curtains of Solomon.[c]
Do not stare at me because I am dark,
    because I am darkened by the sun.
My mother’s sons were angry with me
    and made me take care of the vineyards;(M)
    my own vineyard I had to neglect.
Tell me, you whom I love,
    where you graze your flock
    and where you rest your sheep(N) at midday.
Why should I be like a veiled(O) woman
    beside the flocks of your friends?

Friends

If you do not know, most beautiful of women,(P)
    follow the tracks of the sheep
and graze your young goats
    by the tents of the shepherds.

He

I liken you, my darling, to a mare
    among Pharaoh’s chariot horses.(Q)
10 Your cheeks(R) are beautiful with earrings,
    your neck with strings of jewels.(S)
11 We will make you earrings of gold,
    studded with silver.

She

12 While the king was at his table,
    my perfume spread its fragrance.(T)
13 My beloved is to me a sachet of myrrh(U)
    resting between my breasts.
14 My beloved(V) is to me a cluster of henna(W) blossoms
    from the vineyards of En Gedi.(X)

He

15 How beautiful(Y) you are, my darling!
    Oh, how beautiful!
    Your eyes are doves.(Z)

She

16 How handsome you are, my beloved!(AA)
    Oh, how charming!
    And our bed is verdant.

He

17 The beams of our house are cedars;(AB)
    our rafters are firs.

Footnotes

  1. Song of Songs 1:2 The main male and female speakers (identified primarily on the basis of the gender of the relevant Hebrew forms) are indicated by the captions He and She respectively. The words of others are marked Friends. In some instances the divisions and their captions are debatable.
  2. Song of Songs 1:4 The Hebrew is masculine singular.
  3. Song of Songs 1:5 Or Salma