Nyimbo ya Solomoni 1
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Mkazi
2 Undipsompsone ndi milomo yako
chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;
dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.
Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!
Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.
Abwenzi
Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,
tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.
Mkazi
Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,
inu akazi a ku Yerusalemu,
ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,
ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,
ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.
Alongo anga anandikwiyira
ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;
munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako
ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.
Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere
pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Abwenzi
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,
ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa
ndipo udyetse ana ambuzi
pambali pa matenti a abusa.
Mwamuna
9 Iwe bwenzi langa,
uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,
khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide
zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Mkazi
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,
mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,
kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,
ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Mwamuna
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,
maso ako ali ngati nkhunda.
Mkazi
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!
Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Mwamuna
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,
phaso lake ndi la mtengo wa payini.
Song of Songs 1
New International Version
1 Solomon’s Song of Songs.(A)
She[a]
2 Let him kiss me with the kisses of his mouth—
for your love(B) is more delightful than wine.(C)
3 Pleasing is the fragrance of your perfumes;(D)
your name(E) is like perfume poured out.
No wonder the young women(F) love you!
4 Take me away with you—let us hurry!
Let the king bring me into his chambers.(G)
Friends
She
How right they are to adore you!
5 Dark am I, yet lovely,(J)
daughters of Jerusalem,(K)
dark like the tents of Kedar,(L)
like the tent curtains of Solomon.[c]
6 Do not stare at me because I am dark,
because I am darkened by the sun.
My mother’s sons were angry with me
and made me take care of the vineyards;(M)
my own vineyard I had to neglect.
7 Tell me, you whom I love,
where you graze your flock
and where you rest your sheep(N) at midday.
Why should I be like a veiled(O) woman
beside the flocks of your friends?
Friends
8 If you do not know, most beautiful of women,(P)
follow the tracks of the sheep
and graze your young goats
by the tents of the shepherds.
He
9 I liken you, my darling, to a mare
among Pharaoh’s chariot horses.(Q)
10 Your cheeks(R) are beautiful with earrings,
your neck with strings of jewels.(S)
11 We will make you earrings of gold,
studded with silver.
She
12 While the king was at his table,
my perfume spread its fragrance.(T)
13 My beloved is to me a sachet of myrrh(U)
resting between my breasts.
14 My beloved(V) is to me a cluster of henna(W) blossoms
from the vineyards of En Gedi.(X)
He
She
16 How handsome you are, my beloved!(AA)
Oh, how charming!
And our bed is verdant.
He
17 The beams of our house are cedars;(AB)
our rafters are firs.
Footnotes
- Song of Songs 1:2 The main male and female speakers (identified primarily on the basis of the gender of the relevant Hebrew forms) are indicated by the captions He and She respectively. The words of others are marked Friends. In some instances the divisions and their captions are debatable.
- Song of Songs 1:4 The Hebrew is masculine singular.
- Song of Songs 1:5 Or Salma
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.