Add parallel Print Page Options

Za Kulumbira

30 Mose anawuza Aisraeli onse zonse zimene Yehova anamulamula. Iye anati, “Zimene Yehova walamula ndi izi: Munthu wamwamuna ngati walonjeza kwa Yehova kapena kulumbira kuti adzachita zimene walumbirazo, asaphwanye mawuwo koma ayenera kuchita chilichonse chimene wanena.

“Pamene munthu wamkazi amene akukhalabe mʼnyumba ya abambo ake alumbira kwa Yehova kuti adzachita zimene walonjeza pa ubwana wake, abambo ake namva kulumbira kwakeko kapena kulonjeza kwake kuti adzachitadi, ndipo abambo akewo wosayankhula kanthu, mkaziyo achitedi zomwe analumbirazo. Ayenera kudzachita zonse zimene walonjeza zija. Koma ngati abambo akewo amva kulumbira kwake ndi kumukaniza, palibe lamulo lomukakamiza mkaziyo kuchita zimene walonjeza. Yehova adzamukhululukira chifukwa abambo ake anamukaniza.

“Ngati akwatiwa atalumbira kale kapena ngati alonjeza mofulumira ndi pakamwa pake, mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma wosanenapo kanthu, mkaziyo achitedi zomwe walumbirazo. Achite ndithu zomwe walonjeza zija. Koma ngati mwamuna wake amuletsa atamva kulumbira kwakeko, pamenepo amumasula mayiyo ku zimene analumbira komanso ku zimene analonjeza mosaganiza bwinozo ndipo Yehova adzamukhululukira.

“Mayi wamasiye kapena wosiyidwa ukwati akalumbira kapena kulonjeza kuti adzachita kanthu kalikonse, ayenera kukachitadi.

10 “Koma ngati mayi wokwatiwa alumbira nalonjeza kuti adzachitadi zimene walonjeza, 11 mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma osayankhulapo kanthu, osamuletsa, ayenera kuchitadi zonse zimene walumbira ndi zonse zimene walonjeza. 12 Koma ngati mwamuna wake amva ndi kumuletsa kuti asachite zomwe walumbirazo, palibe lamulo lomukakamiza mayiyo kuchita zomwe walumbirazo kapenanso zimene walonjeza. Popeza mwamuna wake wamuletsa, Yehova adzamukhululukira mayiyo. 13 Mwamuna wake ali ndi mphamvu zovomereza kapena kukana zimene mayiyo walumbira kapena zimene walonjeza zokhudza kudzilanga yekha. 14 Ndipo ngati mmawa mwake ndi masiku otsatira mwamuna wake sanenapo kanthu atamva zimenezi, mayiyo achitedi zimene walumbira kapena zimene walonjeza. Mwamunayo wavomereza zimenezo, chifukwa sanamuwuze kanthu mayiyo pa tsiku limene anamva akulonjeza kapena kulumbira. 15 Koma ngati mwamunayo amukaniza patapita kanthawi atazimva kale, iyeyo ndiye wochimwa mʼmalo mwa mayiyo.”

16 Awa ndiwo malamulo amene Yehova analamula Mose za mwamuna ndi mkazi wake, ndiponso abambo ndi mwana wawo wamkazi amene akanali mtsikana wokhalabe mʼnyumba ya abambo akewo.

Vows

30 [a]Moses said to the heads of the tribes of Israel:(A) “This is what the Lord commands: When a man makes a vow to the Lord or takes an oath to obligate himself by a pledge, he must not break his word but must do everything he said.(B)

“When a young woman still living in her father’s household makes a vow to the Lord or obligates herself by a pledge and her father hears about her vow or pledge but says nothing to her, then all her vows and every pledge by which she obligated herself will stand.(C) But if her father forbids her(D) when he hears about it, none of her vows or the pledges by which she obligated herself will stand; the Lord will release her because her father has forbidden her.

“If she marries after she makes a vow(E) or after her lips utter a rash promise by which she obligates herself and her husband hears about it but says nothing to her, then her vows or the pledges by which she obligated herself will stand. But if her husband(F) forbids her when he hears about it, he nullifies the vow that obligates her or the rash promise by which she obligates herself, and the Lord will release her.(G)

“Any vow or obligation taken by a widow or divorced woman will be binding on her.

10 “If a woman living with her husband makes a vow or obligates herself by a pledge under oath 11 and her husband hears about it but says nothing to her and does not forbid her, then all her vows or the pledges by which she obligated herself will stand. 12 But if her husband nullifies them when he hears about them, then none of the vows or pledges that came from her lips will stand.(H) Her husband has nullified them, and the Lord will release her. 13 Her husband may confirm or nullify any vow she makes or any sworn pledge to deny herself.[b] 14 But if her husband says nothing to her about it from day to day, then he confirms all her vows or the pledges binding on her. He confirms them by saying nothing to her when he hears about them. 15 If, however, he nullifies them(I) some time after he hears about them, then he must bear the consequences of her wrongdoing.”

16 These are the regulations the Lord gave Moses concerning relationships between a man and his wife, and between a father and his young daughter still living at home.

Footnotes

  1. Numbers 30:1 In Hebrew texts 30:1-16 is numbered 30:2-17.
  2. Numbers 30:13 Or to fast