Add parallel Print Page Options

Uthenga Woyamba wa Balaamu

23 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.

Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”

Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”

Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu. Ndipo Balaamu ananena uthenga wake:

“Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu,
    mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa.
Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga,
    pita nyoza Israeli.’
Ndingatemberere bwanji
    amene Mulungu sanawatemberere?
Ndinganyoze bwanji
    amene Yehova sanawanyoze?
Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu,
    ndikuwaona kuchokera pa zitunda.
Ndikuona anthu okhala pawokha,
    osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi,
    kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli?
Lekeni ndife imfa ya oyera mtima,
    ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”

11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”

12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”

Uthenga Wachiwiri wa Balaamu

13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.” 14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”

16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”

17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”

18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake:

“Nyamuka Balaki ndipo tamvera;
    Undimvere iwe mwana wa Zipori.
19 Mulungu si munthu kuti aname,
    kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake.
Kodi amayankhula koma osachita?
    Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
20 Wandilamula kuti ndidalitse,
    Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.

21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo,
    sanaone chovuta mu Israeli.
Yehova Mulungu wawo ali nawo:
    mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto,
    ali ndi mphamvu ngati za njati.
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo,
    palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli.
Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti,
    ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi;
    adzuka okha ngati mkango waumuna
umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira
    ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”

25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!

26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’ ”

Uthenga Wachitatu wa Balaamu

27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.” 28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.

29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.

Balaam’s First Message

23 Balaam said, “Build me seven altars here, and prepare seven bulls and seven rams(A) for me.” Balak did as Balaam said, and the two of them offered a bull and a ram on each altar.(B)

Then Balaam said to Balak, “Stay here beside your offering while I go aside. Perhaps the Lord will come to meet with me.(C) Whatever he reveals to me I will tell you.” Then he went off to a barren height.

God met with him,(D) and Balaam said, “I have prepared seven altars, and on each altar I have offered a bull and a ram.”

The Lord put a word in Balaam’s mouth(E) and said, “Go back to Balak and give him this word.”(F)

So he went back to him and found him standing beside his offering, with all the Moabite officials.(G) Then Balaam(H) spoke his message:(I)

“Balak brought me from Aram,(J)
    the king of Moab from the eastern mountains.(K)
‘Come,’ he said, ‘curse Jacob for me;
    come, denounce Israel.’(L)
How can I curse
    those whom God has not cursed?(M)
How can I denounce
    those whom the Lord has not denounced?(N)
From the rocky peaks I see them,
    from the heights I view them.(O)
I see a people who live apart
    and do not consider themselves one of the nations.(P)
10 Who can count the dust of Jacob(Q)
    or number even a fourth of Israel?
Let me die the death of the righteous,(R)
    and may my final end be like theirs!(S)

11 Balak said to Balaam, “What have you done to me? I brought you to curse my enemies,(T) but you have done nothing but bless them!”(U)

12 He answered, “Must I not speak what the Lord puts in my mouth?”(V)

Balaam’s Second Message

13 Then Balak said to him, “Come with me to another place(W) where you can see them; you will not see them all but only the outskirts of their camp.(X) And from there, curse them for me.(Y) 14 So he took him to the field of Zophim on the top of Pisgah,(Z) and there he built seven altars and offered a bull and a ram on each altar.(AA)

15 Balaam said to Balak, “Stay here beside your offering while I meet with him over there.”

16 The Lord met with Balaam and put a word in his mouth(AB) and said, “Go back to Balak and give him this word.”

17 So he went to him and found him standing beside his offering, with the Moabite officials.(AC) Balak asked him, “What did the Lord say?”

18 Then he spoke his message:(AD)

“Arise, Balak, and listen;
    hear me, son of Zippor.(AE)
19 God is not human,(AF) that he should lie,(AG)
    not a human being, that he should change his mind.(AH)
Does he speak and then not act?
    Does he promise(AI) and not fulfill?
20 I have received a command to bless;(AJ)
    he has blessed,(AK) and I cannot change it.(AL)

21 “No misfortune is seen in Jacob,(AM)
    no misery observed[a] in Israel.(AN)
The Lord their God is with them;(AO)
    the shout of the King(AP) is among them.
22 God brought them out of Egypt;(AQ)
    they have the strength of a wild ox.(AR)
23 There is no divination against[b] Jacob,
    no evil omens(AS) against[c] Israel.
It will now be said of Jacob
    and of Israel, ‘See what God has done!’
24 The people rise like a lioness;(AT)
    they rouse themselves like a lion(AU)
that does not rest till it devours its prey
    and drinks the blood(AV) of its victims.”

25 Then Balak said to Balaam, “Neither curse them at all nor bless them at all!”

26 Balaam answered, “Did I not tell you I must do whatever the Lord says?”(AW)

Balaam’s Third Message

27 Then Balak said to Balaam, “Come, let me take you to another place.(AX) Perhaps it will please God to let you curse them for me(AY) from there.” 28 And Balak took Balaam to the top of Peor,(AZ) overlooking the wasteland.

29 Balaam said, “Build me seven altars here, and prepare seven bulls and seven rams for me.” 30 Balak did as Balaam had said, and offered a bull and a ram on each altar.(BA)

Footnotes

  1. Numbers 23:21 Or He has not looked on Jacob’s offenses / or on the wrongs found
  2. Numbers 23:23 Or in
  3. Numbers 23:23 Or in