Add parallel Print Page Options

Madzi Ochokera Mʼthanthwe

20 Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.

Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova! Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno? Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”

Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera. Yehova anati kwa Mose, “Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”

Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira. 10 Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?” 11 Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.

12 Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”

13 Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.

Aedomu Akaniza Njira Aisraeli

14 Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti,

“Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera. 15 Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo, 16 koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.”

“Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu. 17 Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”

18 Koma Edomu anayankha kuti,

“Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”

19 Aisraeli anayankha kuti,

“Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”

20 Koma Edomu anayankhanso kuti,

“Musadutse.”

Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu. 21 Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.

Aaroni Amwalira

22 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori. 23 Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, 24 “Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba. 25 Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori. 26 Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”

27 Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona. 28 Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko, 29 ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.

Water From the Rock

20 In the first month the whole Israelite community arrived at the Desert of Zin,(A) and they stayed at Kadesh.(B) There Miriam(C) died and was buried.

Now there was no water(D) for the community,(E) and the people gathered in opposition(F) to Moses and Aaron. They quarreled(G) with Moses and said, “If only we had died when our brothers fell dead(H) before the Lord!(I) Why did you bring the Lord’s community into this wilderness,(J) that we and our livestock should die here?(K) Why did you bring us up out of Egypt to this terrible place? It has no grain or figs, grapevines or pomegranates.(L) And there is no water to drink!(M)

Moses and Aaron went from the assembly to the entrance to the tent of meeting(N) and fell facedown,(O) and the glory of the Lord(P) appeared to them. The Lord said to Moses, “Take the staff,(Q) and you and your brother Aaron gather the assembly together. Speak to that rock before their eyes and it will pour out its water.(R) You will bring water out of the rock for the community so they and their livestock can drink.”

So Moses took the staff(S) from the Lord’s presence,(T) just as he commanded him. 10 He and Aaron gathered the assembly together(U) in front of the rock and Moses said to them, “Listen, you rebels, must we bring you water out of this rock?”(V) 11 Then Moses raised his arm and struck the rock twice with his staff. Water(W) gushed out, and the community and their livestock drank.

12 But the Lord said to Moses and Aaron, “Because you did not trust in me enough to honor me as holy(X) in the sight of the Israelites, you will not bring this community into the land I give them.”(Y)

13 These were the waters of Meribah,[a](Z) where the Israelites quarreled(AA) with the Lord and where he was proved holy among them.(AB)

Edom Denies Israel Passage

14 Moses sent messengers from Kadesh(AC) to the king of Edom,(AD) saying:

“This is what your brother Israel says: You know(AE) about all the hardships(AF) that have come on us. 15 Our ancestors went down into Egypt,(AG) and we lived there many years.(AH) The Egyptians mistreated(AI) us and our ancestors, 16 but when we cried out to the Lord, he heard our cry(AJ) and sent an angel(AK) and brought us out of Egypt.(AL)

“Now we are here at Kadesh, a town on the edge of your territory.(AM) 17 Please let us pass through your country. We will not go through any field or vineyard, or drink water from any well. We will travel along the King’s Highway and not turn to the right or to the left until we have passed through your territory.(AN)

18 But Edom(AO) answered:

“You may not pass through here; if you try, we will march out and attack you with the sword.(AP)

19 The Israelites replied:

“We will go along the main road, and if we or our livestock(AQ) drink any of your water, we will pay for it.(AR) We only want to pass through on foot—nothing else.”

20 Again they answered:

“You may not pass through.(AS)

Then Edom(AT) came out against them with a large and powerful army. 21 Since Edom refused to let them go through their territory,(AU) Israel turned away from them.(AV)

The Death of Aaron

22 The whole Israelite community set out from Kadesh(AW) and came to Mount Hor.(AX) 23 At Mount Hor, near the border of Edom,(AY) the Lord said to Moses and Aaron, 24 “Aaron will be gathered to his people.(AZ) He will not enter the land I give the Israelites, because both of you rebelled against my command(BA) at the waters of Meribah.(BB) 25 Get Aaron and his son Eleazar and take them up Mount Hor.(BC) 26 Remove Aaron’s garments(BD) and put them on his son Eleazar, for Aaron will be gathered to his people;(BE) he will die there.”

27 Moses did as the Lord commanded: They went up Mount Hor(BF) in the sight of the whole community. 28 Moses removed Aaron’s garments and put them on his son Eleazar.(BG) And Aaron died there(BH) on top of the mountain. Then Moses and Eleazar came down from the mountain, 29 and when the whole community learned that Aaron had died,(BI) all the Israelites mourned for him(BJ) thirty days.

Footnotes

  1. Numbers 20:13 Meribah means quarreling.