Add parallel Print Page Options

Phulusa ndi Madzi Oyeretsera

19 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: “Lamulo limene Yehova wapereka ndi ili: Uzani Aisraeli kuti abweretse ngʼombe yayikazi yofiira yopanda chilema chilichonse imenenso sinakhalepo pa goli. Muyipereke kwa Eliezara, wansembe ndipo apite nayo kunja kwa msasa. Iphedwe iye ali pomwepo. Ndipo Eliezara wansembe atengeko ena mwa magazi a ngʼombeyo ndi chala chake ndi kuwaza kasanu nʼkawiri ku tsogolo kwa tenti ya msonkhano. Wansembeyo akuona, ngʼombeyo ayiwotche chikopa chake, mnofu wake, magazi ake ndi zamʼkati zake. Wansembe atenge mtengo wamkungudza, hisope ndi kansalu kofiira ndipo aponye zimenezo pakati pa moto umene akuwotchera ngʼombeyo. Zitatha izi, wansembeyo ayenera kuchapa zovala zake ndiponso asambe ndi madzi. Iye angathe kupita ku msasa, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Munthu amene amawotcha ngʼombeyo ayeneranso kuchapa zovala zake ndi kusamba ndi madzi. Iyenso adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.

“Munthu amene ndi woyeretsedwa achotse phulusa la ngʼombeyo ndi kuliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa msasa. Aisraeli adzasunge phulusalo kuti azikaligwiritsa ntchito polithira mʼmadzi woyeretsera ndi wochotsera tchimo. 10 Munthu wochotsa phulusa la ngʼombeyo ayeneranso kuchapa zovala zake. Iyenso adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo.

11 “Aliyense wokhudza mtembo wa munthu wina aliyense adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri. 12 Adziyeretse yekha ndi madzi pa tsiku lachitatu ndi pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ndipo adzayeretsedwa. Koma ngati sadziyeretsa yekha pa tsiku la chitatu ndi lachisanu ndi chiwiri sadzakhala woyeretsedwa. 13 Aliyense amene akhudza mtembo wa munthu nʼkulephera kudziyeretsa yekha, ndiye kuti wadetsa Nyumba ya Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa Aisraeli. Iye ndi wodetsedwa chifukwa sanamuwaze madzi oyeretsa; kudetsedwa kwake kukhalabe pa iyeyo.

14 “Pamene munthu wamwalira mu tenti, lamulo lomwe ligwire ntchito ndi ili: Aliyense wolowa mu tentimo ndi amene anali momwemo adzakhala odetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, 15 ndiponso chiwiya chilichonse chopanda chivundikiro chidzakhala chodetsedwa.

16 “Aliyense wokhudza munthu amene waphedwera kunja ndi lupanga kapena amene wafa ndi imfa ya chilengedwe, kapena aliyense wokhudza fupa la munthu kapena manda, munthu ameneyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri.

17 “Za munthu wodetsedwayo: ikani phulusa lochokera ku nsembe ya chiyeretso mu mtsuko ndi kuthiramo madzi abwino. 18 Tsono munthu woyeretsedwa atenge hisope, amuviyike mʼmadzi ndi kuwaza tentiyo ndi zipangizo zonse, pamodzi ndi anthu anali mʼmenemo. Ayenera kuwazanso aliyense wakhudza fupa kapena, munthu wochita kuphedwa, kapena amene wafa ndi imfa ya chilengedwe kapenanso amene wakhudza manda. 19 Munthu woyeretsedwa ndiye awaze munthu wodetsedwayo pa tsiku lachitatu ndi pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amuyeretse. Munthu amene akuyeretsedwayo ayenera kuchapa zovala zake ndi kusamba ndi madzi, ndipo madzulo ake adzakhala woyeretsedwa. 20 Koma ngati munthu wodetsedwayo sadziyeretsa yekha, ndiye kuti ayenera kuchotsedwa pakati pa gulu chifukwa anadetsa malo wopatulika a Yehova, popeza sanawazidwe madzi oyeretsa ndiye kuti ndi wodetsedwa. 21 Ili ndi lamulo lokhazikika kwa iwo.

“Munthu amene amawaza madzi oyeretsawo ayenera kuchapa zovala zake ndipo yense wokhudza madzi oyeretserawo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. 22 Chilichonse chimene munthu wodetsedwayo achikhudze chidzakhala chodetsedwa ndiponso aliyense wochikhudza adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.”

The Water of Cleansing

19 The Lord said to Moses and Aaron: “This is a requirement of the law that the Lord has commanded: Tell the Israelites to bring you a red heifer(A) without defect or blemish(B) and that has never been under a yoke.(C) Give it to Eleazar(D) the priest; it is to be taken outside the camp(E) and slaughtered in his presence. Then Eleazar the priest is to take some of its blood on his finger and sprinkle(F) it seven times toward the front of the tent of meeting. While he watches, the heifer is to be burned—its hide, flesh, blood and intestines.(G) The priest is to take some cedar wood, hyssop(H) and scarlet wool(I) and throw them onto the burning heifer. After that, the priest must wash his clothes and bathe himself with water.(J) He may then come into the camp, but he will be ceremonially unclean till evening. The man who burns it must also wash his clothes and bathe with water, and he too will be unclean till evening.

“A man who is clean shall gather up the ashes of the heifer(K) and put them in a ceremonially clean place(L) outside the camp. They are to be kept by the Israelite community for use in the water of cleansing;(M) it is for purification from sin.(N) 10 The man who gathers up(O) the ashes of the heifer must also wash his clothes, and he too will be unclean till evening.(P) This will be a lasting ordinance(Q) both for the Israelites and for the foreigners residing among them.(R)

11 “Whoever touches a human corpse(S) will be unclean for seven days.(T) 12 They must purify themselves with the water on the third day and on the seventh day;(U) then they will be clean. But if they do not purify themselves on the third and seventh days, they will not be clean.(V) 13 If they fail to purify themselves after touching a human corpse,(W) they defile the Lord’s tabernacle.(X) They must be cut off from Israel.(Y) Because the water of cleansing has not been sprinkled on them, they are unclean;(Z) their uncleanness remains on them.

14 “This is the law that applies when a person dies in a tent: Anyone who enters the tent and anyone who is in it will be unclean for seven days, 15 and every open container(AA) without a lid fastened on it will be unclean.

16 “Anyone out in the open who touches someone who has been killed with a sword or someone who has died a natural death,(AB) or anyone who touches a human bone(AC) or a grave,(AD) will be unclean for seven days.(AE)

17 “For the unclean person, put some ashes(AF) from the burned purification offering into a jar and pour fresh water(AG) over them. 18 Then a man who is ceremonially clean is to take some hyssop,(AH) dip it in the water and sprinkle(AI) the tent and all the furnishings and the people who were there. He must also sprinkle anyone who has touched a human bone or a grave(AJ) or anyone who has been killed or anyone who has died a natural death. 19 The man who is clean is to sprinkle(AK) those who are unclean on the third and seventh days, and on the seventh day he is to purify them.(AL) Those who are being cleansed must wash their clothes(AM) and bathe with water, and that evening they will be clean. 20 But if those who are unclean do not purify themselves, they must be cut off from the community, because they have defiled(AN) the sanctuary of the Lord.(AO) The water of cleansing has not been sprinkled on them, and they are unclean.(AP) 21 This is a lasting ordinance(AQ) for them.

“The man who sprinkles the water of cleansing must also wash his clothes, and anyone who touches the water of cleansing will be unclean till evening. 22 Anything that an unclean(AR) person touches becomes unclean, and anyone who touches it becomes unclean till evening.”