Add parallel Print Page Options

Malipenga Asiliva

10 Yehova anawuza Mose kuti, “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa. Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano. Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe. Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka. Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo. Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.

“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse. Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu. 10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”

Aisraeli Achoka ku Sinai

11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni. 12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani. 13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.

14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu. 15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara, 16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni. 17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.

18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri. 19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai, 20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi. 21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.

22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo. 23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase. 24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.

25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai. 26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri, 27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani. 28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.

29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”

30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”

31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu. 32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”

33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo. 34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.

35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti,

“Dzukani, Inu Yehova!
    Adani anu abalalike;
    Odana nanu athawe pamaso panu.

36 “Pamene likupumula, ankanena kuti,

“Bwererani, Inu Yehova,
    ku chinamtindi cha Aisraeli.”

The Silver Trumpets

10 The Lord said to Moses: “Make two trumpets(A) of hammered silver, and use them for calling the community(B) together and for having the camps set out.(C) When both are sounded, the whole community is to assemble before you at the entrance to the tent of meeting. If only one is sounded, the leaders(D)—the heads of the clans of Israel—are to assemble before you. When a trumpet blast is sounded, the tribes camping on the east are to set out.(E) At the sounding of a second blast, the camps on the south are to set out.(F) The blast will be the signal for setting out. To gather the assembly, blow the trumpets,(G) but not with the signal for setting out.(H)

“The sons of Aaron, the priests, are to blow the trumpets. This is to be a lasting ordinance for you and the generations to come.(I) When you go into battle in your own land against an enemy who is oppressing you,(J) sound a blast on the trumpets.(K) Then you will be remembered(L) by the Lord your God and rescued from your enemies.(M) 10 Also at your times of rejoicing—your appointed festivals and New Moon feasts(N)—you are to sound the trumpets(O) over your burnt offerings(P) and fellowship offerings,(Q) and they will be a memorial for you before your God. I am the Lord your God.(R)

The Israelites Leave Sinai

11 On the twentieth day of the second month of the second year,(S) the cloud lifted(T) from above the tabernacle of the covenant law.(U) 12 Then the Israelites set out from the Desert of Sinai and traveled from place to place until the cloud came to rest in the Desert of Paran.(V) 13 They set out, this first time, at the Lord’s command through Moses.(W)

14 The divisions of the camp of Judah went first, under their standard.(X) Nahshon son of Amminadab(Y) was in command. 15 Nethanel son of Zuar was over the division of the tribe(Z) of Issachar,(AA) 16 and Eliab son of Helon(AB) was over the division of the tribe of Zebulun.(AC) 17 Then the tabernacle was taken down, and the Gershonites and Merarites, who carried it, set out.(AD)

18 The divisions of the camp of Reuben(AE) went next, under their standard.(AF) Elizur son of Shedeur(AG) was in command. 19 Shelumiel son of Zurishaddai was over the division of the tribe of Simeon,(AH) 20 and Eliasaph son of Deuel was over the division of the tribe of Gad.(AI) 21 Then the Kohathites(AJ) set out, carrying the holy things.(AK) The tabernacle was to be set up before they arrived.(AL)

22 The divisions of the camp of Ephraim(AM) went next, under their standard. Elishama son of Ammihud(AN) was in command. 23 Gamaliel son of Pedahzur was over the division of the tribe of Manasseh,(AO) 24 and Abidan son of Gideoni was over the division of the tribe of Benjamin.(AP)

25 Finally, as the rear guard(AQ) for all the units, the divisions of the camp of Dan set out under their standard. Ahiezer son of Ammishaddai(AR) was in command. 26 Pagiel son of Okran was over the division of the tribe of Asher,(AS) 27 and Ahira son of Enan was over the division of the tribe of Naphtali.(AT) 28 This was the order of march for the Israelite divisions as they set out.

29 Now Moses said to Hobab(AU) son of Reuel(AV) the Midianite, Moses’ father-in-law,(AW) “We are setting out for the place about which the Lord said, ‘I will give it to you.’(AX) Come with us and we will treat you well, for the Lord has promised good things to Israel.”

30 He answered, “No, I will not go;(AY) I am going back to my own land and my own people.(AZ)

31 But Moses said, “Please do not leave us. You know where we should camp in the wilderness, and you can be our eyes.(BA) 32 If you come with us, we will share with you(BB) whatever good things the Lord gives us.(BC)

33 So they set out(BD) from the mountain of the Lord and traveled for three days. The ark of the covenant of the Lord(BE) went before them during those three days to find them a place to rest.(BF) 34 The cloud of the Lord was over them by day when they set out from the camp.(BG)

35 Whenever the ark set out, Moses said,

“Rise up,(BH) Lord!
    May your enemies be scattered;(BI)
    may your foes flee before you.(BJ)(BK)

36 Whenever it came to rest, he said,

“Return,(BL) Lord,
    to the countless thousands of Israel.(BM)