Add parallel Print Page Options

Kalembera

Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa:

Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,

Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,

Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,

Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,

Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,

10 Mwa ana a Yosefe:

kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi;

kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;

11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,

12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,

13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,

14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,

15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”

16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.

17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, 18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi 19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:

20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.

22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.

24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.

26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.

28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.

30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.

32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe:

Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.

34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.

36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.

38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.

40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.

42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali:

Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.

44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. 45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. 46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.

47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. 48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, 49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. 50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. 51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. 52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. 53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”

54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

The Census

The Lord spoke to Moses in the tent of meeting(A) in the Desert of Sinai(B) on the first day of the second month(C) of the second year after the Israelites came out of Egypt.(D) He said: “Take a census(E) of the whole Israelite community by their clans and families,(F) listing every man by name,(G) one by one. You and Aaron(H) are to count according to their divisions all the men in Israel who are twenty years old or more(I) and able to serve in the army.(J) One man from each tribe,(K) each of them the head of his family,(L) is to help you.(M) These are the names(N) of the men who are to assist you:

from Reuben,(O) Elizur son of Shedeur;(P)

from Simeon,(Q) Shelumiel son of Zurishaddai;(R)

from Judah,(S) Nahshon son of Amminadab;(T)

from Issachar,(U) Nethanel son of Zuar;(V)

from Zebulun,(W) Eliab son of Helon;(X)

10 from the sons of Joseph:

from Ephraim,(Y) Elishama son of Ammihud;(Z)

from Manasseh,(AA) Gamaliel son of Pedahzur;(AB)

11 from Benjamin,(AC) Abidan son of Gideoni;(AD)

12 from Dan,(AE) Ahiezer son of Ammishaddai;(AF)

13 from Asher,(AG) Pagiel son of Okran;(AH)

14 from Gad,(AI) Eliasaph son of Deuel;(AJ)

15 from Naphtali,(AK) Ahira son of Enan.(AL)

16 These were the men appointed from the community, the leaders(AM) of their ancestral tribes.(AN) They were the heads of the clans of Israel.(AO)

17 Moses and Aaron took these men whose names had been specified, 18 and they called the whole community together on the first day of the second month.(AP) The people registered their ancestry(AQ) by their clans and families,(AR) and the men twenty years old or more(AS) were listed by name, one by one, 19 as the Lord commanded Moses. And so he counted(AT) them in the Desert of Sinai:

20 From the descendants of Reuben(AU) the firstborn son(AV) of Israel:

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, one by one, according to the records of their clans and families. 21 The number from the tribe of Reuben(AW) was 46,500.

22 From the descendants of Simeon:(AX)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were counted and listed by name, one by one, according to the records of their clans and families. 23 The number from the tribe of Simeon was 59,300.(AY)

24 From the descendants of Gad:(AZ)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 25 The number from the tribe of Gad(BA) was 45,650.

26 From the descendants of Judah:(BB)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 27 The number from the tribe of Judah(BC) was 74,600.

28 From the descendants of Issachar:(BD)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 29 The number from the tribe of Issachar(BE) was 54,400.(BF)

30 From the descendants of Zebulun:(BG)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 31 The number from the tribe of Zebulun was 57,400.(BH)

32 From the sons of Joseph:(BI)

From the descendants of Ephraim:(BJ)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 33 The number from the tribe of Ephraim(BK) was 40,500.

34 From the descendants of Manasseh:(BL)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 35 The number from the tribe of Manasseh was 32,200.

36 From the descendants of Benjamin:(BM)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 37 The number from the tribe of Benjamin(BN) was 35,400.

38 From the descendants of Dan:(BO)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 39 The number from the tribe of Dan was 62,700.(BP)

40 From the descendants of Asher:(BQ)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 41 The number from the tribe of Asher(BR) was 41,500.

42 From the descendants of Naphtali:(BS)

All the men twenty years old or more who were able to serve in the army were listed by name, according to the records of their clans and families. 43 The number from the tribe of Naphtali(BT) was 53,400.(BU)

44 These were the men counted by Moses and Aaron(BV) and the twelve leaders of Israel, each one representing his family. 45 All the Israelites twenty years old or more(BW) who were able to serve in Israel’s army were counted according to their families.(BX) 46 The total number was 603,550.(BY)

47 The ancestral tribe of the Levites,(BZ) however, was not counted(CA) along with the others. 48 The Lord had said to Moses: 49 “You must not count the tribe of Levi or include them in the census of the other Israelites. 50 Instead, appoint the Levites to be in charge of the tabernacle(CB) of the covenant law(CC)—over all its furnishings(CD) and everything belonging to it. They are to carry the tabernacle and all its furnishings; they are to take care of it and encamp around it. 51 Whenever the tabernacle(CE) is to move,(CF) the Levites are to take it down, and whenever the tabernacle is to be set up, the Levites shall do it.(CG) Anyone else who approaches it is to be put to death.(CH) 52 The Israelites are to set up their tents by divisions, each of them in their own camp under their standard.(CI) 53 The Levites, however, are to set up their tents around the tabernacle(CJ) of the covenant law so that my wrath will not fall(CK) on the Israelite community. The Levites are to be responsible for the care of the tabernacle of the covenant law.(CL)

54 The Israelites did all this just as the Lord commanded Moses.