Add parallel Print Page Options

Nzika Zatsopano za mu Yerusalemu

11 Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo. Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.

Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu. Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini.

Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa:

Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi. Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni. Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.

Nazi zidzukulu za Benjamini:

Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya. Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928. Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.

10 Ansembe anali awa:

Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini; 11 Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu, 12 ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya, 13 ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri 14 ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.

15 Alevi anali awa:

Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni. 16 Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu. 17 Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni. 18 Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.

19 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.

20 Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.

21 Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.

22 Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu. 23 Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.

24 Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.

25 Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake, 26 ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti, 27 Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo. 28 Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo, 29 ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti, 30 Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.

31 Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake, 32 ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya, 33 ku Hazori, Rama ndi Gitaimu, 34 ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati, 35 ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.

36 Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

The New Residents of Jerusalem(A)

11 Now the leaders of the people settled in Jerusalem. The rest of the people cast lots to bring one out of every ten of them to live in Jerusalem,(B) the holy city,(C) while the remaining nine were to stay in their own towns.(D) The people commended all who volunteered to live in Jerusalem.

These are the provincial leaders who settled in Jerusalem (now some Israelites, priests, Levites, temple servants and descendants of Solomon’s servants lived in the towns of Judah, each on their own property in the various towns,(E) while other people from both Judah and Benjamin(F) lived in Jerusalem):(G)

From the descendants of Judah:

Athaiah son of Uzziah, the son of Zechariah, the son of Amariah, the son of Shephatiah, the son of Mahalalel, a descendant of Perez; and Maaseiah son of Baruch, the son of Kol-Hozeh, the son of Hazaiah, the son of Adaiah, the son of Joiarib, the son of Zechariah, a descendant of Shelah. The descendants of Perez who lived in Jerusalem totaled 468 men of standing.

From the descendants of Benjamin:

Sallu son of Meshullam, the son of Joed, the son of Pedaiah, the son of Kolaiah, the son of Maaseiah, the son of Ithiel, the son of Jeshaiah, and his followers, Gabbai and Sallai—928 men. Joel son of Zikri was their chief officer, and Judah son of Hassenuah was over the New Quarter of the city.

10 From the priests:

Jedaiah; the son of Joiarib; Jakin; 11 Seraiah(H) son of Hilkiah, the son of Meshullam, the son of Zadok, the son of Meraioth, the son of Ahitub,(I) the official in charge of the house of God, 12 and their associates, who carried on work for the temple—822 men; Adaiah son of Jeroham, the son of Pelaliah, the son of Amzi, the son of Zechariah, the son of Pashhur, the son of Malkijah, 13 and his associates, who were heads of families—242 men; Amashsai son of Azarel, the son of Ahzai, the son of Meshillemoth, the son of Immer, 14 and his[a] associates, who were men of standing—128. Their chief officer was Zabdiel son of Haggedolim.

15 From the Levites:

Shemaiah son of Hasshub, the son of Azrikam, the son of Hashabiah, the son of Bunni; 16 Shabbethai(J) and Jozabad,(K) two of the heads of the Levites, who had charge of the outside work of the house of God; 17 Mattaniah(L) son of Mika, the son of Zabdi, the son of Asaph,(M) the director who led in thanksgiving and prayer; Bakbukiah, second among his associates; and Abda son of Shammua, the son of Galal, the son of Jeduthun.(N) 18 The Levites in the holy city(O) totaled 284.

19 The gatekeepers:

Akkub, Talmon and their associates, who kept watch at the gates—172 men.

20 The rest of the Israelites, with the priests and Levites, were in all the towns of Judah, each on their ancestral property.

21 The temple servants(P) lived on the hill of Ophel, and Ziha and Gishpa were in charge of them.

22 The chief officer of the Levites in Jerusalem was Uzzi son of Bani, the son of Hashabiah, the son of Mattaniah,(Q) the son of Mika. Uzzi was one of Asaph’s descendants, who were the musicians responsible for the service of the house of God. 23 The musicians(R) were under the king’s orders, which regulated their daily activity.

24 Pethahiah son of Meshezabel, one of the descendants of Zerah(S) son of Judah, was the king’s agent in all affairs relating to the people.

25 As for the villages with their fields, some of the people of Judah lived in Kiriath Arba(T) and its surrounding settlements, in Dibon(U) and its settlements, in Jekabzeel and its villages, 26 in Jeshua, in Moladah,(V) in Beth Pelet,(W) 27 in Hazar Shual,(X) in Beersheba(Y) and its settlements, 28 in Ziklag,(Z) in Mekonah and its settlements, 29 in En Rimmon, in Zorah,(AA) in Jarmuth,(AB) 30 Zanoah,(AC) Adullam(AD) and their villages, in Lachish(AE) and its fields, and in Azekah(AF) and its settlements. So they were living all the way from Beersheba(AG) to the Valley of Hinnom.

31 The descendants of the Benjamites from Geba(AH) lived in Mikmash,(AI) Aija, Bethel(AJ) and its settlements, 32 in Anathoth,(AK) Nob(AL) and Ananiah, 33 in Hazor,(AM) Ramah(AN) and Gittaim,(AO) 34 in Hadid, Zeboim(AP) and Neballat, 35 in Lod and Ono,(AQ) and in Ge Harashim.

36 Some of the divisions of the Levites of Judah settled in Benjamin.

Footnotes

  1. Nehemiah 11:14 Most Septuagint manuscripts; Hebrew their