Add parallel Print Page Options

Tsoka la Ninive

Tsoka kwa mzinda wopha anthu,
    mzinda wodzaza ndi mabodza,
mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo,
    mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
Kulira kwa zikwapu,
    mkokomo wa mikombero,
kufuwula kwa akavalo
    ndiponso phokoso la magaleta!
Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo,
    kungʼanima kwa malupanga
    ndi kunyezimira kwa mikondo!
Anthu ambiri ophedwa,
    milumilu ya anthu akufa,
mitembo yosawerengeka,
    anthu akupunthwa pa mitemboyo.
Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere,
    wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga,
amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake,
    ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.

Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Ine ndikutsutsana nawe.
    Ndidzakuvula chovala chako.
Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako
    ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
Ndidzakuthira zonyansa,
    ndidzakuchititsa manyazi
    ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati,
    ‘Ninive wasanduka bwinja,
    adzamulira ndani?’
Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”

Kodi ndiwe wopambana Tebesi,
    mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo,
    wozunguliridwa ndi madzi?
Mtsinjewo unali chitetezo chake,
    madziwo anali linga lake.
Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto,
    Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa
    ndipo anapita ku ukapolo.
Ana ake anawaphwanyitsa pansi
    mʼmisewu yonse ya mu mzindamo.
Anachita maere ogawana anthu ake otchuka,
    ndipo anthu ake onse amphamvu
    anamangidwa ndi maunyolo.
11 Iwenso Ninive udzaledzera;
    udzabisala
    ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.

12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu
    yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha;
    pamene agwedeza mitengoyo,
    nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
13 Tayangʼana ankhondo ako,
    onse ali ngati akazi!
Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako;
    moto wapsereza mipiringidzo yake.

14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu,
    limbitsani chitetezo chanu!
Pondani dothi,
    ikani mʼchikombole,
    konzani khoma la njerwa!
15 Kumeneko moto udzakupserezani;
    lupanga lidzakukanthani
    ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala.
Chulukanani ngati ziwala,
    chulukanani ngati dzombe!
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu
    mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga,
koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko
    ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
17 Akalonga ako ali ngati dzombe,
    akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe
    limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira,
koma pamene dzuwa latuluka limawuluka,
    ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.

18 Iwe mfumu ya ku Asiriya,
    abusa ako agona tulo;
    anthu ako olemekezeka amwalira.
Anthu ako amwazikira ku mapiri
    popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
19 Palibe chimene chingachize bala lako;
    chilonda chako sichingapole.
Aliyense amene amamva za iwe
    amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako,
kodi alipo amene sanazilawepo
    nkhanza zako zosatha?

Woe to Nineveh

Woe to the city of blood,(A)
    full of lies,(B)
full of plunder,
    never without victims!
The crack of whips,
    the clatter of wheels,
galloping horses
    and jolting chariots!
Charging cavalry,
    flashing swords
    and glittering spears!
Many casualties,
    piles of dead,
bodies without number,
    people stumbling over the corpses(C)
all because of the wanton lust of a prostitute,
    alluring, the mistress of sorceries,(D)
who enslaved nations by her prostitution(E)
    and peoples by her witchcraft.

“I am against(F) you,” declares the Lord Almighty.
    “I will lift your skirts(G) over your face.
I will show the nations your nakedness(H)
    and the kingdoms your shame.
I will pelt you with filth,(I)
    I will treat you with contempt(J)
    and make you a spectacle.(K)
All who see you will flee(L) from you and say,
    ‘Nineveh(M) is in ruins(N)—who will mourn for her?’(O)
    Where can I find anyone to comfort(P) you?”

Are you better than(Q) Thebes,(R)
    situated on the Nile,(S)
    with water around her?
The river was her defense,
    the waters her wall.
Cush[a](T) and Egypt were her boundless strength;
    Put(U) and Libya(V) were among her allies.
10 Yet she was taken captive(W)
    and went into exile.
Her infants were dashed(X) to pieces
    at every street corner.
Lots(Y) were cast for her nobles,
    and all her great men were put in chains.(Z)
11 You too will become drunk;(AA)
    you will go into hiding(AB)
    and seek refuge from the enemy.

12 All your fortresses are like fig trees
    with their first ripe fruit;(AC)
when they are shaken,
    the figs(AD) fall into the mouth of the eater.
13 Look at your troops—
    they are all weaklings.(AE)
The gates(AF) of your land
    are wide open to your enemies;
    fire has consumed the bars of your gates.(AG)

14 Draw water for the siege,(AH)
    strengthen your defenses!(AI)
Work the clay,
    tread the mortar,
    repair the brickwork!
15 There the fire(AJ) will consume you;
    the sword(AK) will cut you down—
    they will devour you like a swarm of locusts.
Multiply like grasshoppers,
    multiply like locusts!(AL)
16 You have increased the number of your merchants
    till they are more numerous than the stars in the sky,
but like locusts(AM) they strip the land
    and then fly away.
17 Your guards are like locusts,(AN)
    your officials like swarms of locusts
    that settle in the walls on a cold day—
but when the sun appears they fly away,
    and no one knows where.

18 King of Assyria, your shepherds[b] slumber;(AO)
    your nobles lie down to rest.(AP)
Your people are scattered(AQ) on the mountains
    with no one to gather them.
19 Nothing can heal you;(AR)
    your wound is fatal.
All who hear the news about you
    clap their hands(AS) at your fall,
for who has not felt
    your endless cruelty?(AT)

Footnotes

  1. Nahum 3:9 That is, the upper Nile region
  2. Nahum 3:18 That is, rulers