Add parallel Print Page Options

Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

Yehova ndi Mulungu wansanje
ndiponso wobwezera;
    Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.
Yehova amabwezera adani ake
    ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;
    ndipo sadzalola kuti munthu
    wolakwa asalangidwe.
Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,
    ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Amalamulira nyanja ndipo imawuma;
amawumitsa mitsinje yonse.
Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma
    ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Mapiri amagwedera pamaso pake
ndipo zitunda zimasungunuka.
Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,
    dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?
    Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?
Ukali wake ukuyaka ngati moto;
    matanthwe akunyeka pamaso pake.

Yehova ndi wabwino,
    ndiye kothawirako nthawi ya masautso.
Amasamalira amene amamudalira,
koma ndi madzi achigumula choopsa
Iye adzawononga adani ake (Ninive);
    adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova
    adzachiwononga kotheratu;
    msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga
    ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;
    adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,
    wofuna kuchitira Yehova chiwembu,
    amene amapereka uphungu woyipa.
12 Yehova akuti,
“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,
    kaya iwowo ndi ambiri,
    koma adzawonongedwa ndi kutheratu.
Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,
    sindidzakuzunzanso.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako
    ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,
    “Sudzakhala ndi zidzukulu
    zimene zidzadziwike ndi dzina lako.
Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba
    amene ali mʼnyumba ya milungu yako.
Ine ndidzakukumbira manda
    chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 Taonani, pa phiripo,
    mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,
    amene akulengeza za mtendere!
Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu
    ndipo kwaniritsani malumbiro anu.
Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;
    iwo adzawonongedwa kotheratu.

A prophecy(A) concerning Nineveh.(B) The book of the vision(C) of Nahum the Elkoshite.

The Lord’s Anger Against Nineveh

The Lord is a jealous(D) and avenging God;
    the Lord takes vengeance(E) and is filled with wrath.
The Lord takes vengeance on his foes
    and vents his wrath against his enemies.(F)
The Lord is slow to anger(G) but great in power;
    the Lord will not leave the guilty unpunished.(H)
His way is in the whirlwind(I) and the storm,(J)
    and clouds(K) are the dust of his feet.
He rebukes(L) the sea and dries it up;(M)
    he makes all the rivers run dry.
Bashan and Carmel(N) wither
    and the blossoms of Lebanon fade.
The mountains quake(O) before him
    and the hills melt away.(P)
The earth trembles(Q) at his presence,
    the world and all who live in it.(R)
Who can withstand(S) his indignation?
    Who can endure(T) his fierce anger?(U)
His wrath is poured out like fire;(V)
    the rocks are shattered(W) before him.

The Lord is good,(X)
    a refuge in times of trouble.(Y)
He cares for(Z) those who trust in him,(AA)
    but with an overwhelming flood(AB)
he will make an end of Nineveh;
    he will pursue his foes into the realm of darkness.

Whatever they plot(AC) against the Lord
    he will bring[a] to an end;
    trouble will not come a second time.
10 They will be entangled among thorns(AD)
    and drunk(AE) from their wine;
    they will be consumed like dry stubble.[b](AF)
11 From you, Nineveh, has one come forth
    who plots evil against the Lord
    and devises wicked plans.

12 This is what the Lord says:

“Although they have allies and are numerous,
    they will be destroyed(AG) and pass away.
Although I have afflicted you, Judah,
    I will afflict you no more.(AH)
13 Now I will break their yoke(AI) from your neck
    and tear your shackles away.”(AJ)

14 The Lord has given a command concerning you, Nineveh:
    “You will have no descendants to bear your name.(AK)
I will destroy the images(AL) and idols
    that are in the temple of your gods.
I will prepare your grave,(AM)
    for you are vile.”

15 Look, there on the mountains,
    the feet of one who brings good news,(AN)
    who proclaims peace!(AO)
Celebrate your festivals,(AP) Judah,
    and fulfill your vows.
No more will the wicked invade you;(AQ)
    they will be completely destroyed.[c]

Footnotes

  1. Nahum 1:9 Or What do you foes plot against the Lord? / He will bring it
  2. Nahum 1:10 The meaning of the Hebrew for this verse is uncertain.
  3. Nahum 1:15 In Hebrew texts this verse (1:15) is numbered 2:1.