Mlaliki 4
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Matsoka ndi Mavuto a Moyo Uno
4 Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:
ndinaona misozi ya anthu opsinjika,
ndipo iwo alibe owatonthoza;
mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo
ndipo iwonso analibe owatonthoza.
2 Ndipo ndinanena kuti akufa,
amene anafa kale,
ndi osangalala kuposa amoyo,
amene akanalibe ndi moyo.
3 Koma wopambana onsewa
ndi amene sanabadwe,
amene sanaone zoyipa
zimene chimachitika pansi pano.
4 Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 Chitsiru chimangoti manja ake lobodo
ndi kudzipha chokha ndi njala.
6 Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,
kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto,
ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.
7 Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 Panali munthu amene anali yekhayekha;
analibe mwana kapena mʼbale.
Ntchito yake yolemetsa sinkatha,
ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.
Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?
Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?”
Izinso ndi zopandapake,
zosasangalatsa!
9 Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,
chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:
10 Ngati winayo agwa,
mnzakeyo adzamudzutsa.
Koma tsoka kwa munthu amene agwa
ndipo alibe wina woti amudzutse!
11 Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.
Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?
12 Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,
koma anthu awiri akhoza kudziteteza.
Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.
Kutukuka Nʼkopandapake
13 Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo. 14 Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo. 15 Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu. 16 Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.
Ecclesiastes 4
New International Version
Oppression, Toil, Friendlessness
4 Again I looked and saw all the oppression(A) that was taking place under the sun:
I saw the tears of the oppressed—
and they have no comforter;
power was on the side of their oppressors—
and they have no comforter.(B)
2 And I declared that the dead,(C)
who had already died,
are happier than the living,
who are still alive.(D)
3 But better than both
is the one who has never been born,(E)
who has not seen the evil
that is done under the sun.(F)
4 And I saw that all toil and all achievement spring from one person’s envy of another. This too is meaningless, a chasing after the wind.(G)
5 Fools fold their hands(H)
and ruin themselves.
6 Better one handful with tranquillity
than two handfuls with toil(I)
and chasing after the wind.
7 Again I saw something meaningless under the sun:
8 There was a man all alone;
he had neither son nor brother.
There was no end to his toil,
yet his eyes were not content(J) with his wealth.
“For whom am I toiling,” he asked,
“and why am I depriving myself of enjoyment?”
This too is meaningless—
a miserable business!
9 Two are better than one,
because they have a good return for their labor:
10 If either of them falls down,
one can help the other up.
But pity anyone who falls
and has no one to help them up.
11 Also, if two lie down together, they will keep warm.
But how can one keep warm alone?
12 Though one may be overpowered,
two can defend themselves.
A cord of three strands is not quickly broken.
Advancement Is Meaningless
13 Better a poor but wise youth than an old but foolish king who no longer knows how to heed a warning. 14 The youth may have come from prison to the kingship, or he may have been born in poverty within his kingdom. 15 I saw that all who lived and walked under the sun followed the youth, the king’s successor. 16 There was no end to all the people who were before them. But those who came later were not pleased with the successor. This too is meaningless, a chasing after the wind.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.