Add parallel Print Page Options

Chilichonse Chili ndi Nthawi

Chinthu chilichonse chili ndi nthawi yake,
    ndi nyengo yake yomwe anayika Mulungu:

    Nthawi yobadwa ndi nthawi yomwalira,
    nthawi yodzala ndi nthawi yokolola.
    Nthawi yakupha ndi nthawi yochiritsa,
    nthawi yogwetsa ndi nthawi yomanga.
    Nthawi yomva chisoni ndi nthawi yosangalala,
    nthawi yolira maliro ndi nthawi yovina.
    Nthawi yotaya miyala ndi nthawi yokundika miyala,
    nthawi yokumbatirana ndi nthawi yoleka kukumbatirana.
    Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna,
    nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.
    Nthawi yongʼamba ndi nthawi yosoka,
    nthawi yokhala chete ndi nthawi yoyankhula.
    Nthawi yokondana ndi nthawi yodana,
    nthawi ya nkhondo ndi nthawi ya mtendere.

Kodi wantchito amapeza phindu lanji pa ntchito yake yolemetsa? 10 Ine ndinaona chipsinjo chimene Mulungu anayika pa anthu. 11 Iye anapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthawi yake. Anayika nzeru zamuyaya mʼmitima ya anthu; komabe anthuwo sangathe kuzindikira zomwe Mulungu wachita kuyambira pa chiyambi mpaka chimaliziro. 12 Ine ndikudziwa kuti palibenso kanthu kabwino kwa anthu kopambana kusangalala ndi kuchita zabwino pamene ali ndi moyo. 13 Ndi mphatso ya Mulungu kwa munthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ndi ntchito zake zolemetsa. 14 Ndikudziwa kuti chilichonse chimene Mulungu amachita chidzakhala mpaka muyaya; palibe zimene zingawonjezedwe kapena kuchotsedwa. Mulungu amazichita kuti anthu azimuopa.

15 Chilichonse chimene chilipo chinalipo kale,
    ndipo chimene chidzakhalapo chinalipo poyamba;
    Mulungu amabwezanso zakale zimene zinapita kuti zichitikenso.

16 Ndipo ndinaona chinthu chinanso pansi pano:

ku malo achiweruzo, kuyipa mtima kuli komweko,
    ku malo achilungamo, kuyipa mtima kuli komweko.

17 Ndinalingalira mu mtima mwanga kuti;

“Mulungu adzaweruza
    olungama pamodzi ndi oyipa omwe,
pakuti anayika nthawi yochitikira chinthu chilichonse,
    nthawi ya ntchito iliyonse.”

18 Ndinalingaliranso kuti, “Kunena za anthu, Mulungu amawayesa ndi cholinga choti awaonetse kuti iwo ali ngati nyama. 19 Zimene zimachitikira munthu, zomwezonso zimachitikira nyama; chinthu chimodzi chomwecho chimachitikira onse: Monga munthu amafa momwemonso nyama imafa. Zonsezi zimapuma mpweya umodzimodzi omwewo; munthu saposa nyama. Zonsezi ndi zopandapake. 20 Zonse zimapita kumodzimodzi; zonsezi zimachokera ku fumbi, ndipo zimabwereranso ku fumbi komweko. 21 Kodi ndani amene amadziwa ngati mzimu wa munthu umakwera kumwamba, ndipo mzimu wa nyama umatsikira kunsi kwa dziko?”

22 Kotero ndinaona kuti palibe chinthu chabwino kwa munthu kuposa kuti munthu azisangalala ndi ntchito yake, pakuti ichi ndiye chake chenicheni. Pakuti ndani amene angamubweretse kuti adzaone zimene zidzamuchitikira iye akadzamwalira?

A Time for Everything

There is a time(A) for everything,
    and a season for every activity under the heavens:

    a time to be born and a time to die,
    a time to plant and a time to uproot,(B)
    a time to kill(C) and a time to heal,
    a time to tear down and a time to build,
    a time to weep and a time to laugh,
    a time to mourn and a time to dance,
    a time to scatter stones and a time to gather them,
    a time to embrace and a time to refrain from embracing,
    a time to search and a time to give up,
    a time to keep and a time to throw away,
    a time to tear and a time to mend,
    a time to be silent(D) and a time to speak,
    a time to love and a time to hate,
    a time for war and a time for peace.

What do workers gain from their toil?(E) 10 I have seen the burden God has laid on the human race.(F) 11 He has made everything beautiful in its time.(G) He has also set eternity in the human heart; yet[a] no one can fathom(H) what God has done from beginning to end.(I) 12 I know that there is nothing better for people than to be happy and to do good while they live. 13 That each of them may eat and drink,(J) and find satisfaction(K) in all their toil—this is the gift of God.(L) 14 I know that everything God does will endure forever; nothing can be added to it and nothing taken from it. God does it so that people will fear him.(M)

15 Whatever is has already been,(N)
    and what will be has been before;(O)
    and God will call the past to account.[b]

16 And I saw something else under the sun:

In the place of judgment—wickedness was there,
    in the place of justice—wickedness was there.

17 I said to myself,

“God will bring into judgment(P)
    both the righteous and the wicked,
for there will be a time for every activity,
    a time to judge every deed.”(Q)

18 I also said to myself, “As for humans, God tests them so that they may see that they are like the animals.(R) 19 Surely the fate of human beings(S) is like that of the animals; the same fate awaits them both: As one dies, so dies the other. All have the same breath[c]; humans have no advantage over animals. Everything is meaningless. 20 All go to the same place; all come from dust, and to dust all return.(T) 21 Who knows if the human spirit rises upward(U) and if the spirit of the animal goes down into the earth?”

22 So I saw that there is nothing better for a person than to enjoy their work,(V) because that is their lot.(W) For who can bring them to see what will happen after them?

Footnotes

  1. Ecclesiastes 3:11 Or also placed ignorance in the human heart, so that
  2. Ecclesiastes 3:15 Or God calls back the past
  3. Ecclesiastes 3:19 Or spirit