Add parallel Print Page Options

Zosangalatsa Nʼzopandapake

Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake. “Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?” Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.

Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa. Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse. Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija. Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu. Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.

10 Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna;
    mtima wanga sindinawumane zokondweretsa.
Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse,
    ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.
11 Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga,
    ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze,
zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe,
    palibe chomwe ndinapindula pansi pano.

Nzeru ndi Uchitsiru Nʼzopandapake

12 Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani,
    komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani.
Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani
    choposa chimene chinachitidwa kale?
13 Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru,
    monga momwe kuwala kumapambanira mdima.
14 Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo,
    pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli;
koma ndinazindikira kuti chomwe
    chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.

15 Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga,

“Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine.
    Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?”
Ndinati mu mtima mwanga,
    “Ichinso ndi chopandapake.”
16 Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali;
    mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika.
Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!

Kugwira Ntchito Nʼkopandapake

17 Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe. 18 Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga. 19 Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake. 20 Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano. 21 Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu. 22 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano? 23 Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.

24 Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu, 25 pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo? 26 Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

Pleasures Are Meaningless

I said to myself, “Come now, I will test you with pleasure(A) to find out what is good.” But that also proved to be meaningless. “Laughter,”(B) I said, “is madness. And what does pleasure accomplish?” I tried cheering myself with wine,(C) and embracing folly(D)—my mind still guiding me with wisdom. I wanted to see what was good for people to do under the heavens during the few days of their lives.

I undertook great projects: I built houses for myself(E) and planted vineyards.(F) I made gardens and parks and planted all kinds of fruit trees in them. I made reservoirs to water groves of flourishing trees. I bought male and female slaves and had other slaves(G) who were born in my house. I also owned more herds and flocks than anyone in Jerusalem before me. I amassed silver and gold(H) for myself, and the treasure of kings and provinces.(I) I acquired male and female singers,(J) and a harem[a] as well—the delights of a man’s heart. I became greater by far than anyone in Jerusalem(K) before me.(L) In all this my wisdom stayed with me.

10 I denied myself nothing my eyes desired;
    I refused my heart no pleasure.
My heart took delight in all my labor,
    and this was the reward for all my toil.
11 Yet when I surveyed all that my hands had done
    and what I had toiled to achieve,
everything was meaningless, a chasing after the wind;(M)
    nothing was gained under the sun.(N)

Wisdom and Folly Are Meaningless

12 Then I turned my thoughts to consider wisdom,
    and also madness and folly.(O)
What more can the king’s successor do
    than what has already been done?(P)
13 I saw that wisdom(Q) is better than folly,(R)
    just as light is better than darkness.
14 The wise have eyes in their heads,
    while the fool walks in the darkness;
but I came to realize
    that the same fate overtakes them both.(S)

15 Then I said to myself,

“The fate of the fool will overtake me also.
    What then do I gain by being wise?”(T)
I said to myself,
    “This too is meaningless.”
16 For the wise, like the fool, will not be long remembered;(U)
    the days have already come when both have been forgotten.(V)
Like the fool, the wise too must die!(W)

Toil Is Meaningless

17 So I hated life, because the work that is done under the sun was grievous to me. All of it is meaningless, a chasing after the wind.(X) 18 I hated all the things I had toiled for under the sun, because I must leave them to the one who comes after me.(Y) 19 And who knows whether that person will be wise or foolish?(Z) Yet they will have control over all the fruit of my toil into which I have poured my effort and skill under the sun. This too is meaningless. 20 So my heart began to despair over all my toilsome labor under the sun. 21 For a person may labor with wisdom, knowledge and skill, and then they must leave all they own to another who has not toiled for it. This too is meaningless and a great misfortune. 22 What do people get for all the toil and anxious striving with which they labor under the sun?(AA) 23 All their days their work is grief and pain;(AB) even at night their minds do not rest.(AC) This too is meaningless.

24 A person can do nothing better than to eat and drink(AD) and find satisfaction in their own toil.(AE) This too, I see, is from the hand of God,(AF) 25 for without him, who can eat or find enjoyment?(AG) 26 To the person who pleases him, God gives wisdom,(AH) knowledge and happiness, but to the sinner he gives the task of gathering and storing up wealth(AI) to hand it over to the one who pleases God.(AJ) This too is meaningless, a chasing after the wind.

Footnotes

  1. Ecclesiastes 2:8 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.