Add parallel Print Page Options

12 Uzikumbukira mlengi wako
    masiku a unyamata wako,
masiku oyipa asanafike,
    nthawi isanafike pamene udzanena kuti,
    “Izi sizikundikondweretsa.”
Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala,
    mwezi ndi nyenyezi zidzada.
    Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
Nthawi imene manja ako adzanjenjemera,
    miyendo yako idzafowoka,
pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka,
    ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
Makutu ako adzatsekeka,
    ndipo sudzamva phokoso lakunja;
sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo
    kapena kulira kwa mbalame mmawa.
Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera,
    amaopa kuyenda mʼmisewu;
Mutu umatuwa kuti mbuu,
    amayenda modzikoka ngati ziwala
    ndipo chilakolako chimatheratu.
Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya
    ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.

Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke,
    kapena mbale yagolide isanasweke;
mtsuko usanasweke ku kasupe,
    kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera,
    mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.

“Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki.
    “Zonse ndi zopandapake!”

Mawu Otsiriza

Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri. 10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.

11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi. 12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi.

Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.

13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa:
    uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake,
pakuti umenewu ndiwo udindo
    wa anthu onse.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse,
    kuphatikizanso zinthu zonse zobisika,
    kaya zabwino kapena zoyipa.

12 Remember(A) your Creator
    in the days of your youth,
before the days of trouble(B) come
    and the years approach when you will say,
    “I find no pleasure in them”—
before the sun and the light
    and the moon and the stars grow dark,
    and the clouds return after the rain;
when the keepers of the house tremble,
    and the strong men stoop,
when the grinders cease because they are few,
    and those looking through the windows grow dim;
when the doors to the street are closed
    and the sound of grinding fades;
when people rise up at the sound of birds,
    but all their songs grow faint;(C)
when people are afraid of heights
    and of dangers in the streets;
when the almond tree blossoms
    and the grasshopper drags itself along
    and desire no longer is stirred.
Then people go to their eternal home(D)
    and mourners(E) go about the streets.

Remember him—before the silver cord is severed,
    and the golden bowl is broken;
before the pitcher is shattered at the spring,
    and the wheel broken at the well,
and the dust returns(F) to the ground it came from,
    and the spirit returns to God(G) who gave it.(H)

“Meaningless! Meaningless!” says the Teacher.[a](I)
    “Everything is meaningless!(J)

The Conclusion of the Matter

Not only was the Teacher wise, but he also imparted knowledge to the people. He pondered and searched out and set in order many proverbs.(K) 10 The Teacher(L) searched to find just the right words, and what he wrote was upright and true.(M)

11 The words of the wise are like goads, their collected sayings like firmly embedded nails(N)—given by one shepherd.[b] 12 Be warned, my son, of anything in addition to them.

Of making many books there is no end, and much study wearies the body.(O)

13 Now all has been heard;
    here is the conclusion of the matter:
Fear God(P) and keep his commandments,(Q)
    for this is the duty of all mankind.(R)
14 For God will bring every deed into judgment,(S)
    including every hidden thing,(T)
    whether it is good or evil.

Footnotes

  1. Ecclesiastes 12:8 Or the leader of the assembly; also in verses 9 and 10
  2. Ecclesiastes 12:11 Or Shepherd