Mlaliki 12
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
12 Uzikumbukira mlengi wako
masiku a unyamata wako,
masiku oyipa asanafike,
nthawi isanafike pamene udzanena kuti,
“Izi sizikundikondweretsa.”
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala,
mwezi ndi nyenyezi zidzada.
Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera,
miyendo yako idzafowoka,
pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka,
ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
4 Makutu ako adzatsekeka,
ndipo sudzamva phokoso lakunja;
sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo
kapena kulira kwa mbalame mmawa.
5 Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera,
amaopa kuyenda mʼmisewu;
Mutu umatuwa kuti mbuu,
amayenda modzikoka ngati ziwala
ndipo chilakolako chimatheratu.
Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya
ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
6 Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke,
kapena mbale yagolide isanasweke;
mtsuko usanasweke ku kasupe,
kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
7 Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera,
mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
8 “Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki.
“Zonse ndi zopandapake!”
Mawu Otsiriza
9 Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri. 10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi. 12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi.
Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa:
uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake,
pakuti umenewu ndiwo udindo
wa anthu onse.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse,
kuphatikizanso zinthu zonse zobisika,
kaya zabwino kapena zoyipa.
Ecclesiastes 12
New International Version
12 Remember(A) your Creator
in the days of your youth,
before the days of trouble(B) come
and the years approach when you will say,
“I find no pleasure in them”—
2 before the sun and the light
and the moon and the stars grow dark,
and the clouds return after the rain;
3 when the keepers of the house tremble,
and the strong men stoop,
when the grinders cease because they are few,
and those looking through the windows grow dim;
4 when the doors to the street are closed
and the sound of grinding fades;
when people rise up at the sound of birds,
but all their songs grow faint;(C)
5 when people are afraid of heights
and of dangers in the streets;
when the almond tree blossoms
and the grasshopper drags itself along
and desire no longer is stirred.
Then people go to their eternal home(D)
and mourners(E) go about the streets.
6 Remember him—before the silver cord is severed,
and the golden bowl is broken;
before the pitcher is shattered at the spring,
and the wheel broken at the well,
7 and the dust returns(F) to the ground it came from,
and the spirit returns to God(G) who gave it.(H)
The Conclusion of the Matter
9 Not only was the Teacher wise, but he also imparted knowledge to the people. He pondered and searched out and set in order many proverbs.(K) 10 The Teacher(L) searched to find just the right words, and what he wrote was upright and true.(M)
11 The words of the wise are like goads, their collected sayings like firmly embedded nails(N)—given by one shepherd.[b] 12 Be warned, my son, of anything in addition to them.
Of making many books there is no end, and much study wearies the body.(O)
Footnotes
- Ecclesiastes 12:8 Or the leader of the assembly; also in verses 9 and 10
- Ecclesiastes 12:11 Or Shepherd
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.