Mlaliki 10
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
10 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira,
choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino,
koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu,
zochita zake ndi zopanda nzeru
ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
4 Ngati wolamulira akukwiyira,
usachoke pa ntchito yako;
kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano,
kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba,
pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo,
pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha;
amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo;
amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha
yosanoledwa,
pamafunika mphamvu zambiri potema,
koma luso limabweretsa chipambano.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka
ngati njokayo yakuluma kale.
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa,
koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa;
potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu.
Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo,
ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa;
ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana,
ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka
ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake,
kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka;
ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu,
ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo,
koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako,
kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako,
pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako
nʼkukafotokoza zomwe wanena.
Ecclesiastes 10
New International Version
10 As dead flies give perfume a bad smell,
so a little folly(A) outweighs wisdom and honor.
2 The heart of the wise inclines to the right,
but the heart of the fool to the left.
3 Even as fools walk along the road,
they lack sense
and show everyone(B) how stupid they are.
4 If a ruler’s anger rises against you,
do not leave your post;(C)
calmness can lay great offenses to rest.(D)
5 There is an evil I have seen under the sun,
the sort of error that arises from a ruler:
6 Fools are put in many high positions,(E)
while the rich occupy the low ones.
7 I have seen slaves on horseback,
while princes go on foot like slaves.(F)
8 Whoever digs a pit may fall into it;(G)
whoever breaks through a wall may be bitten by a snake.(H)
9 Whoever quarries stones may be injured by them;
whoever splits logs may be endangered by them.(I)
10 If the ax is dull
and its edge unsharpened,
more strength is needed,
but skill will bring success.
11 If a snake bites before it is charmed,
the charmer receives no fee.(J)
12 Words from the mouth of the wise are gracious,(K)
but fools are consumed by their own lips.(L)
13 At the beginning their words are folly;
at the end they are wicked madness—
14 and fools multiply words.(M)
No one knows what is coming—
who can tell someone else what will happen after them?(N)
15 The toil of fools wearies them;
they do not know the way to town.
16 Woe to the land whose king was a servant[a](O)
and whose princes feast in the morning.
17 Blessed is the land whose king is of noble birth
and whose princes eat at a proper time—
for strength and not for drunkenness.(P)
18 Through laziness, the rafters sag;
because of idle hands, the house leaks.(Q)
19 A feast is made for laughter,
wine(R) makes life merry,
and money is the answer for everything.
20 Do not revile the king(S) even in your thoughts,
or curse the rich in your bedroom,
because a bird in the sky may carry your words,
and a bird on the wing may report what you say.
Footnotes
- Ecclesiastes 10:16 Or king is a child
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.