Add parallel Print Page Options

Nzeru Iposa Zonse

Ananu, mverani malangizo a abambo anu;
    tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.
    Choncho musasiye malangizo anga.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;
    mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,
    “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako,
    usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
    usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
    Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.
    Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;
    ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;
    idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”

10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,
    ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.
    Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;
    ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.
    Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa
    kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;
    uzilambalala nʼkumangopita.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;
    tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi
    ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.

18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha
    kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;
    iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.

20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;
    tchera khutu ku mawu anga.
21 Usayiwale malangizo angawa,
    koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza
    ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu
    pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;
    ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo;
    uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako
    ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere;
    usapite kumene kuli zoyipa.

Get Wisdom at Any Cost

Listen, my sons,(A) to a father’s instruction;(B)
    pay attention and gain understanding.(C)
I give you sound learning,
    so do not forsake my teaching.
For I too was a son to my father,
    still tender, and cherished by my mother.
Then he taught me, and he said to me,
    “Take hold(D) of my words with all your heart;
    keep my commands, and you will live.(E)
Get wisdom,(F) get understanding;
    do not forget my words or turn away from them.
Do not forsake wisdom, and she will protect you;(G)
    love her, and she will watch over you.(H)
The beginning of wisdom is this: Get[a] wisdom.
    Though it cost all(I) you have,[b] get understanding.(J)
Cherish her, and she will exalt you;
    embrace her, and she will honor you.(K)
She will give you a garland to grace your head
    and present you with a glorious crown.(L)

10 Listen, my son,(M) accept what I say,
    and the years of your life will be many.(N)
11 I instruct(O) you in the way of wisdom
    and lead you along straight paths.(P)
12 When you walk, your steps will not be hampered;
    when you run, you will not stumble.(Q)
13 Hold on to instruction, do not let it go;
    guard it well, for it is your life.(R)
14 Do not set foot on the path of the wicked
    or walk in the way of evildoers.(S)
15 Avoid it, do not travel on it;
    turn from it and go on your way.
16 For they cannot rest until they do evil;(T)
    they are robbed of sleep till they make someone stumble.
17 They eat the bread of wickedness
    and drink the wine of violence.(U)

18 The path of the righteous(V) is like the morning sun,(W)
    shining ever brighter till the full light of day.(X)
19 But the way of the wicked is like deep darkness;(Y)
    they do not know what makes them stumble.(Z)

20 My son,(AA) pay attention to what I say;
    turn your ear to my words.(AB)
21 Do not let them out of your sight,(AC)
    keep them within your heart;
22 for they are life to those who find them
    and health to one’s whole body.(AD)
23 Above all else, guard(AE) your heart,
    for everything you do flows from it.(AF)
24 Keep your mouth free of perversity;
    keep corrupt talk far from your lips.
25 Let your eyes(AG) look straight ahead;
    fix your gaze directly before you.
26 Give careful thought to the[c] paths for your feet(AH)
    and be steadfast in all your ways.
27 Do not turn to the right or the left;(AI)
    keep your foot from evil.

Footnotes

  1. Proverbs 4:7 Or Wisdom is supreme; therefore get
  2. Proverbs 4:7 Or wisdom. / Whatever else you get
  3. Proverbs 4:26 Or Make level