Add parallel Print Page Options

Mawu a Aguri

30 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.
    Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;
    ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Sindinaphunzire nzeru,
    ndipo Woyerayo sindimudziwa.
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?
    Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?
Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?
    Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?
Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!
    Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;
    Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,
    kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri
    musandimane zimenezo ndisanafe:
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.
    Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.
    Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,
    nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’
Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,
    potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake
    kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo,
    ndipo sadalitsa amayi awo.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima
    komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,
    amene amakweza zikope modzitukumula.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga
    ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni
moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.
    Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri
    iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,
    zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 Manda, mkazi wosabala,
    nthaka yosakhuta madzi
    ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17 Aliyense amene amanyoza abambo ake,
    ndi kunyozera kumvera amayi ake,
makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso
    ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,
    zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;
    mmene iyendera njoka pa thanthwe;
mmene chiyendera chombo pa nyanja;
    ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:
    Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake
    iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,
    pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu,
    chitsiru chimene chakhuta,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa
    ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,
    komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,
    komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu
    komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 dzombe lilibe mfumu,
    komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja
    komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,
    pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,
    ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,
    ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,
    kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,
    ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,
    ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,
    ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

Sayings of Agur

30 The sayings(A) of Agur son of Jakeh—an inspired utterance.

This man’s utterance to Ithiel:

“I am weary, God,
    but I can prevail.[a]
Surely I am only a brute, not a man;
    I do not have human understanding.
I have not learned wisdom,
    nor have I attained to the knowledge of the Holy One.(B)
Who has gone up(C) to heaven and come down?
    Whose hands(D) have gathered up the wind?
Who has wrapped up the waters(E) in a cloak?(F)
    Who has established all the ends of the earth?
What is his name,(G) and what is the name of his son?
    Surely you know!

“Every word of God is flawless;(H)
    he is a shield(I) to those who take refuge in him.
Do not add(J) to his words,
    or he will rebuke you and prove you a liar.

“Two things I ask of you, Lord;
    do not refuse me before I die:
Keep falsehood and lies far from me;
    give me neither poverty nor riches,
    but give me only my daily bread.(K)
Otherwise, I may have too much and disown(L) you
    and say, ‘Who is the Lord?’(M)
Or I may become poor and steal,
    and so dishonor the name of my God.(N)

10 “Do not slander a servant to their master,
    or they will curse you, and you will pay for it.

11 “There are those who curse their fathers
    and do not bless their mothers;(O)
12 those who are pure in their own eyes(P)
    and yet are not cleansed of their filth;(Q)
13 those whose eyes are ever so haughty,(R)
    whose glances are so disdainful;
14 those whose teeth(S) are swords
    and whose jaws are set with knives(T)
to devour(U) the poor(V) from the earth
    and the needy from among mankind.(W)

15 “The leech has two daughters.
    ‘Give! Give!’ they cry.

“There are three things that are never satisfied,(X)
    four that never say, ‘Enough!’:
16 the grave,(Y) the barren womb,
    land, which is never satisfied with water,
    and fire, which never says, ‘Enough!’

17 “The eye that mocks(Z) a father,
    that scorns an aged mother,
will be pecked out by the ravens of the valley,
    will be eaten by the vultures.(AA)

18 “There are three things that are too amazing for me,
    four that I do not understand:
19 the way of an eagle in the sky,
    the way of a snake on a rock,
the way of a ship on the high seas,
    and the way of a man with a young woman.

20 “This is the way of an adulterous woman:
    She eats and wipes her mouth
    and says, ‘I’ve done nothing wrong.’(AB)

21 “Under three things the earth trembles,
    under four it cannot bear up:
22 a servant who becomes king,(AC)
    a godless fool who gets plenty to eat,
23 a contemptible woman who gets married,
    and a servant who displaces her mistress.

24 “Four things on earth are small,
    yet they are extremely wise:
25 Ants are creatures of little strength,
    yet they store up their food in the summer;(AD)
26 hyraxes(AE) are creatures of little power,
    yet they make their home in the crags;
27 locusts(AF) have no king,
    yet they advance together in ranks;
28 a lizard can be caught with the hand,
    yet it is found in kings’ palaces.

29 “There are three things that are stately in their stride,
    four that move with stately bearing:
30 a lion, mighty among beasts,
    who retreats before nothing;
31 a strutting rooster, a he-goat,
    and a king secure against revolt.[b]

32 “If you play the fool and exalt yourself,
    or if you plan evil,
    clap your hand over your mouth!(AG)
33 For as churning cream produces butter,
    and as twisting the nose produces blood,
    so stirring up anger produces strife.”

Footnotes

  1. Proverbs 30:1 With a different word division of the Hebrew; Masoretic Text utterance to Ithiel, / to Ithiel and Ukal:
  2. Proverbs 30:31 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.