Add parallel Print Page Options

Phindu Lina la Nzeru

Mwana wanga, usayiwale malangizo anga,
    mtima wako usunge malamulo anga.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka
    ndipo udzakhala pa mtendere.

Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere.
    Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda
    ndi kuwalemba pa mtima pako.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino
    pamaso pa Mulungu ndi anthu.

Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse
    ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,
    ndipo Iye adzawongola njira zako.

Usamadzione ngati wa nzeru.
    Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino
    ndi mafupa ako adzakhala olimba.

Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse;
    zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri,
    ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.

11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova,
    ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda,
    monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.

13 Wodala munthu amene wapeza nzeru,
    munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva,
    phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali;
    ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali;
    mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa,
    ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa;
    wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.

19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru.
    Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka
    ndiponso mitambo inagwetsa mvula.

21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino.
    Zimenezi zisakuchokere.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo,
    moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu,
    ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha;
    ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi
    kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima
    ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.

27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino,
    pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti,
    “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa”
    pamene uli nazo tsopano.

29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako,
    amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa
    pamene iye sanakuchitire zoyipa.

31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa
    kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa
    koma amayanjana nawo anthu olungama.

33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa,
    koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza,
    koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu,
    koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

Wisdom Bestows Well-Being

My son,(A) do not forget my teaching,(B)
    but keep my commands in your heart,
for they will prolong your life many years(C)
    and bring you peace and prosperity.(D)

Let love and faithfulness(E) never leave you;
    bind them around your neck,
    write them on the tablet of your heart.(F)
Then you will win favor and a good name
    in the sight of God and man.(G)

Trust in the Lord(H) with all your heart
    and lean not on your own understanding;
in all your ways submit to him,
    and he will make your paths(I) straight.[a](J)

Do not be wise in your own eyes;(K)
    fear the Lord(L) and shun evil.(M)
This will bring health to your body(N)
    and nourishment to your bones.(O)

Honor the Lord with your wealth,
    with the firstfruits(P) of all your crops;
10 then your barns will be filled(Q) to overflowing,
    and your vats will brim over with new wine.(R)

11 My son,(S) do not despise the Lord’s discipline,(T)
    and do not resent his rebuke,
12 because the Lord disciplines those he loves,(U)
    as a father the son he delights in.[b](V)

13 Blessed are those who find wisdom,
    those who gain understanding,
14 for she is more profitable than silver
    and yields better returns than gold.(W)
15 She is more precious than rubies;(X)
    nothing you desire can compare with her.(Y)
16 Long life is in her right hand;(Z)
    in her left hand are riches and honor.(AA)
17 Her ways are pleasant ways,
    and all her paths are peace.(AB)
18 She is a tree of life(AC) to those who take hold of her;
    those who hold her fast will be blessed.(AD)

19 By wisdom(AE) the Lord laid the earth’s foundations,(AF)
    by understanding he set the heavens(AG) in place;
20 by his knowledge the watery depths were divided,
    and the clouds let drop the dew.

21 My son,(AH) do not let wisdom and understanding out of your sight,(AI)
    preserve sound judgment and discretion;
22 they will be life for you,(AJ)
    an ornament to grace your neck.(AK)
23 Then you will go on your way in safety,(AL)
    and your foot will not stumble.(AM)
24 When you lie down,(AN) you will not be afraid;(AO)
    when you lie down, your sleep(AP) will be sweet.
25 Have no fear of sudden disaster
    or of the ruin that overtakes the wicked,
26 for the Lord will be at your side(AQ)
    and will keep your foot(AR) from being snared.(AS)

27 Do not withhold good from those to whom it is due,
    when it is in your power to act.
28 Do not say to your neighbor,
    “Come back tomorrow and I’ll give it to you”—
    when you already have it with you.(AT)
29 Do not plot harm against your neighbor,
    who lives trustfully near you.(AU)
30 Do not accuse anyone for no reason—
    when they have done you no harm.

31 Do not envy(AV) the violent
    or choose any of their ways.

32 For the Lord detests the perverse(AW)
    but takes the upright into his confidence.(AX)
33 The Lord’s curse(AY) is on the house of the wicked,(AZ)
    but he blesses the home of the righteous.(BA)
34 He mocks(BB) proud mockers(BC)
    but shows favor to the humble(BD) and oppressed.
35 The wise inherit honor,
    but fools get only shame.

Footnotes

  1. Proverbs 3:6 Or will direct your paths
  2. Proverbs 3:12 Hebrew; Septuagint loves, / and he chastens everyone he accepts as his child