Miyambo 25
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Miyambo Ina ya Solomoni
25 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu;
ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi,
ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva
ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu;
ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu,
ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,”
kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa.
Chimene wachiona ndi maso ako,
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu
nanga udzachita chiyani pa mapeto pake
ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako,
koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi
ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera
ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide
kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola
kwa anthu amene amutuma;
iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka
ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,
ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,
kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako
ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama,
ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,
kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni
kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira
kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;
ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,
ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula,
chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga
kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali
ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa
ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 Sibwino kudya uchi wambiri,
sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 Munthu amene samatha kudziretsa
ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Proverbs 25
New International Version
More Proverbs of Solomon
25 These are more proverbs(A) of Solomon, compiled by the men of Hezekiah king of Judah:(B)
2 It is the glory of God to conceal a matter;
to search out a matter is the glory of kings.(C)
3 As the heavens are high and the earth is deep,
so the hearts of kings are unsearchable.
4 Remove the dross from the silver,
and a silversmith can produce a vessel;
5 remove wicked officials from the king’s presence,(D)
and his throne will be established(E) through righteousness.(F)
6 Do not exalt yourself in the king’s presence,
and do not claim a place among his great men;
7 it is better for him to say to you, “Come up here,”(G)
than for him to humiliate you before his nobles.
What you have seen with your eyes
8 do not bring[a] hastily to court,
for what will you do in the end
if your neighbor puts you to shame?(H)
9 If you take your neighbor to court,
do not betray another’s confidence,
10 or the one who hears it may shame you
and the charge against you will stand.
11 Like apples[b] of gold in settings of silver(I)
is a ruling rightly given.
12 Like an earring of gold or an ornament of fine gold
is the rebuke of a wise judge to a listening ear.(J)
13 Like a snow-cooled drink at harvest time
is a trustworthy messenger to the one who sends him;
he refreshes the spirit of his master.(K)
14 Like clouds and wind without rain
is one who boasts of gifts never given.
16 If you find honey, eat just enough—
too much of it, and you will vomit.(N)
17 Seldom set foot in your neighbor’s house—
too much of you, and they will hate you.
18 Like a club or a sword or a sharp arrow
is one who gives false testimony against a neighbor.(O)
19 Like a broken tooth or a lame foot
is reliance on the unfaithful in a time of trouble.
20 Like one who takes away a garment on a cold day,
or like vinegar poured on a wound,
is one who sings songs to a heavy heart.
21 If your enemy is hungry, give him food to eat;
if he is thirsty, give him water to drink.
22 In doing this, you will heap burning coals(P) on his head,
and the Lord will reward you.(Q)
23 Like a north wind that brings unexpected rain
is a sly tongue—which provokes a horrified look.
24 Better to live on a corner of the roof
than share a house with a quarrelsome wife.(R)
25 Like cold water to a weary soul
is good news from a distant land.(S)
26 Like a muddied spring or a polluted well
are the righteous who give way to the wicked.
27 It is not good to eat too much honey,(T)
nor is it honorable to search out matters that are too deep.(U)
28 Like a city whose walls are broken through
is a person who lacks self-control.
Footnotes
- Proverbs 25:8 Or nobles / on whom you had set your eyes. / 8 Do not go
- Proverbs 25:11 Or possibly apricots
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.