Add parallel Print Page Options

Miyambo Ina ya Solomoni

25 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.

Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu;
    ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.

Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi,
    ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.

Chotsa zoyipa mʼsiliva
    ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu;
    ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.

Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu,
    ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,”
    kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa.

Chimene wachiona ndi maso ako,
    usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu
nanga udzachita chiyani pa mapeto pake
    ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?

Kamba mlandu ndi mnansi wako,
    koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi
    ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.

11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera
    ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.

12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide
    kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.

13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola
    kwa anthu amene amutuma;
    iye amaziziritsa mtima bwana wake.

14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka
    ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.

15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,
    ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.

16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,
    kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako
    ukawirikiza kupita, udzadana naye.

18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama,
    ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.

19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,
    kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.

20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni
    kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira
    kapena kuthira mchere pa chilonda.

21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;
    ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,
    ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.

23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula,
    chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.

24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga
    kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.

25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali
    ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.

26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa
    ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.

27 Sibwino kudya uchi wambiri,
    sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.

28 Munthu amene samatha kudziretsa
    ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

More Proverbs of Solomon

25 These are more proverbs(A) of Solomon, compiled by the men of Hezekiah king of Judah:(B)

It is the glory of God to conceal a matter;
    to search out a matter is the glory of kings.(C)
As the heavens are high and the earth is deep,
    so the hearts of kings are unsearchable.

Remove the dross from the silver,
    and a silversmith can produce a vessel;
remove wicked officials from the king’s presence,(D)
    and his throne will be established(E) through righteousness.(F)

Do not exalt yourself in the king’s presence,
    and do not claim a place among his great men;
it is better for him to say to you, “Come up here,”(G)
    than for him to humiliate you before his nobles.

What you have seen with your eyes
    do not bring[a] hastily to court,
for what will you do in the end
    if your neighbor puts you to shame?(H)

If you take your neighbor to court,
    do not betray another’s confidence,
10 or the one who hears it may shame you
    and the charge against you will stand.

11 Like apples[b] of gold in settings of silver(I)
    is a ruling rightly given.
12 Like an earring of gold or an ornament of fine gold
    is the rebuke of a wise judge to a listening ear.(J)

13 Like a snow-cooled drink at harvest time
    is a trustworthy messenger to the one who sends him;
    he refreshes the spirit of his master.(K)
14 Like clouds and wind without rain
    is one who boasts of gifts never given.

15 Through patience a ruler can be persuaded,(L)
    and a gentle tongue can break a bone.(M)

16 If you find honey, eat just enough—
    too much of it, and you will vomit.(N)
17 Seldom set foot in your neighbor’s house—
    too much of you, and they will hate you.

18 Like a club or a sword or a sharp arrow
    is one who gives false testimony against a neighbor.(O)
19 Like a broken tooth or a lame foot
    is reliance on the unfaithful in a time of trouble.
20 Like one who takes away a garment on a cold day,
    or like vinegar poured on a wound,
    is one who sings songs to a heavy heart.

21 If your enemy is hungry, give him food to eat;
    if he is thirsty, give him water to drink.
22 In doing this, you will heap burning coals(P) on his head,
    and the Lord will reward you.(Q)

23 Like a north wind that brings unexpected rain
    is a sly tongue—which provokes a horrified look.

24 Better to live on a corner of the roof
    than share a house with a quarrelsome wife.(R)

25 Like cold water to a weary soul
    is good news from a distant land.(S)
26 Like a muddied spring or a polluted well
    are the righteous who give way to the wicked.

27 It is not good to eat too much honey,(T)
    nor is it honorable to search out matters that are too deep.(U)

28 Like a city whose walls are broken through
    is a person who lacks self-control.

Footnotes

  1. Proverbs 25:8 Or nobles / on whom you had set your eyes. / Do not go
  2. Proverbs 25:11 Or possibly apricots