Add parallel Print Page Options

24 Usachitire nsanje anthu oyipa,
    usalakalake kuti uzikhala nawo,
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,
    ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.

Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,
    ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake
    ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.

Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,
    ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.
    Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.

Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;
    chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.

Amene amakonzekera kuchita zoyipa
    adzatchedwa mvundulamadzi.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,
    ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.

10 Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti
    mphamvu yako ndi yochepadi!

11 Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;
    uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”
    kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi?
Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi?
    Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?

13 Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;
    uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;
    ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo,
    ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.

15 Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.
    Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.
    Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.

17 Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.
    Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,
    angaleke kukwiyira mdaniyo.

19 Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa
    kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 paja munthu woyipa alibe tsogolo.
    Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.

21 Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,
    ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.
    Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?

Malangizo Enanso a Anthu Anzeru

23 Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:

Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”
    anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino
    ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.

26 Woyankhula mawu owona
    ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

27 Ugwiriretu ntchito zako zonse,
    makamaka za ku munda
    ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.

28 Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,
    kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;
    ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”

30 Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi
    ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,
    mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,
    ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga
    ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”
    kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 umphawi udzafika pa iwe ngati mbala
    ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

Saying 20

24 Do not envy(A) the wicked,
    do not desire their company;
for their hearts plot violence,(B)
    and their lips talk about making trouble.(C)

Saying 21

By wisdom a house is built,(D)
    and through understanding it is established;
through knowledge its rooms are filled
    with rare and beautiful treasures.(E)

Saying 22

The wise prevail through great power,
    and those who have knowledge muster their strength.
Surely you need guidance to wage war,
    and victory is won through many advisers.(F)

Saying 23

Wisdom is too high for fools;
    in the assembly at the gate they must not open their mouths.

Saying 24

Whoever plots evil
    will be known as a schemer.
The schemes of folly are sin,
    and people detest a mocker.

Saying 25

10 If you falter in a time of trouble,
    how small is your strength!(G)
11 Rescue those being led away to death;
    hold back those staggering toward slaughter.(H)
12 If you say, “But we knew nothing about this,”
    does not he who weighs(I) the heart perceive it?
Does not he who guards your life know it?
    Will he not repay(J) everyone according to what they have done?(K)

Saying 26

13 Eat honey, my son, for it is good;
    honey from the comb is sweet to your taste.
14 Know also that wisdom is like honey for you:
    If you find it, there is a future hope for you,
    and your hope will not be cut off.(L)

Saying 27

15 Do not lurk like a thief near the house of the righteous,
    do not plunder their dwelling place;
16 for though the righteous fall seven times, they rise again,
    but the wicked stumble when calamity strikes.(M)

Saying 28

17 Do not gloat(N) when your enemy falls;
    when they stumble, do not let your heart rejoice,(O)
18 or the Lord will see and disapprove
    and turn his wrath away from them.(P)

Saying 29

19 Do not fret(Q) because of evildoers
    or be envious of the wicked,
20 for the evildoer has no future hope,
    and the lamp of the wicked will be snuffed out.(R)

Saying 30

21 Fear the Lord and the king,(S) my son,
    and do not join with rebellious officials,
22 for those two will send sudden destruction(T) on them,
    and who knows what calamities they can bring?

Further Sayings of the Wise

23 These also are sayings of the wise:(U)

To show partiality(V) in judging is not good:(W)
24 Whoever says to the guilty, “You are innocent,”(X)
    will be cursed by peoples and denounced by nations.
25 But it will go well with those who convict the guilty,
    and rich blessing will come on them.

26 An honest answer
    is like a kiss on the lips.

27 Put your outdoor work in order
    and get your fields ready;
    after that, build your house.

28 Do not testify against your neighbor without cause(Y)
    would you use your lips to mislead?
29 Do not say, “I’ll do to them as they have done to me;
    I’ll pay them back for what they did.”(Z)

30 I went past the field of a sluggard,(AA)
    past the vineyard of someone who has no sense;
31 thorns had come up everywhere,
    the ground was covered with weeds,
    and the stone wall was in ruins.
32 I applied my heart to what I observed
    and learned a lesson from what I saw:
33 A little sleep, a little slumber,
    a little folding of the hands to rest(AB)
34 and poverty will come on you like a thief
    and scarcity like an armed man.(AC)