Miyambo 20
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
20 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola;
aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango;
amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano,
koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera;
kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya,
munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo,
koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino;
odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo,
imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga;
ndilibe tchimo lililonse?”
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo
zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake,
ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona,
zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 Usakonde tulo ungasauke;
khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.”
Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali,
koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;
kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu,
koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu;
ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi.
Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake,
moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba,
sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!”
Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova;
ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova,
tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,”
popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu
anthu oyipa.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova;
imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu;
chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo,
imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa,
ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Proverbs 20
New International Version
2 A king’s wrath strikes terror like the roar of a lion;(E)
those who anger him forfeit their lives.(F)
5 The purposes of a person’s heart are deep waters,(K)
but one who has insight draws them out.
6 Many claim to have unfailing love,
but a faithful person who can find?(L)
10 Differing weights and differing measures—
the Lord detests them both.(S)
11 Even small children are known by their actions,
so is their conduct really pure(T) and upright?
12 Ears that hear and eyes that see—
the Lord has made them both.(U)
13 Do not love sleep or you will grow poor;(V)
stay awake and you will have food to spare.
14 “It’s no good, it’s no good!” says the buyer—
then goes off and boasts about the purchase.
15 Gold there is, and rubies in abundance,
but lips that speak knowledge are a rare jewel.
16 Take the garment of one who puts up security for a stranger;
hold it in pledge(W) if it is done for an outsider.(X)
18 Plans are established by seeking advice;
so if you wage war, obtain guidance.(AA)
19 A gossip betrays a confidence;(AB)
so avoid anyone who talks too much.
20 If someone curses their father or mother,(AC)
their lamp will be snuffed out in pitch darkness.(AD)
21 An inheritance claimed too soon
will not be blessed at the end.
22 Do not say, “I’ll pay you back for this wrong!”(AE)
Wait for the Lord, and he will avenge you.(AF)
23 The Lord detests differing weights,
and dishonest scales do not please him.(AG)
24 A person’s steps are directed(AH) by the Lord.(AI)
How then can anyone understand their own way?(AJ)
25 It is a trap to dedicate something rashly
and only later to consider one’s vows.(AK)
26 A wise king winnows out the wicked;
he drives the threshing wheel over them.(AL)
29 The glory of young men is their strength,
gray hair the splendor of the old.(AQ)
Footnotes
- Proverbs 20:27 Or A person’s words are
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.