Add parallel Print Page Options

18 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha;
    iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.

Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu,
    koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.

Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera.
    Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.

Mawu a munthu ali ngati madzi akuya,
    kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.

Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu;
    kapena kupondereza munthu wosalakwa.

Mawu a chitsiru amautsa mkangano;
    pakamwa pake pamayitana mkwapulo.

Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake,
    ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.

Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma;
    amalowa mʼmimba mwa munthu.

Munthu waulesi pa ntchito yake
    ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.

10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba;
    wolungama amathawiramo napulumuka.

11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba;
    chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.

12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada,
    koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.

13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani,
    umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.

14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda,
    koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.

15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina;
    amafunafuna kudziwa bwino zinthu.

16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira
    yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.

17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye
    mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.

18 Kuchita maere kumathetsa mikangano;
    amalekanitsa okangana amphamvu.

19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba,
    koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.

20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake.
    Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.

21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.
    Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.

22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino
    ndipo Yehova amamukomera mtima.

23 Munthu wosauka amapempha
    koma munthu wolemera amayankha mwaukali.

24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso,
    koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

18 An unfriendly person pursues selfish ends
    and against all sound judgment starts quarrels.

Fools find no pleasure in understanding
    but delight in airing their own opinions.(A)

When wickedness comes, so does contempt,
    and with shame comes reproach.

The words of the mouth are deep waters,(B)
    but the fountain of wisdom is a rushing stream.

It is not good to be partial to the wicked(C)
    and so deprive the innocent of justice.(D)

The lips of fools bring them strife,
    and their mouths invite a beating.(E)

The mouths of fools are their undoing,
    and their lips are a snare(F) to their very lives.(G)

The words of a gossip are like choice morsels;
    they go down to the inmost parts.(H)

One who is slack in his work
    is brother to one who destroys.(I)

10 The name of the Lord is a fortified tower;(J)
    the righteous run to it and are safe.(K)

11 The wealth of the rich is their fortified city;(L)
    they imagine it a wall too high to scale.

12 Before a downfall the heart is haughty,
    but humility comes before honor.(M)

13 To answer before listening—
    that is folly and shame.(N)

14 The human spirit can endure in sickness,
    but a crushed spirit who can bear?(O)

15 The heart of the discerning acquires knowledge,(P)
    for the ears of the wise seek it out.

16 A gift(Q) opens the way
    and ushers the giver into the presence of the great.

17 In a lawsuit the first to speak seems right,
    until someone comes forward and cross-examines.

18 Casting the lot settles disputes(R)
    and keeps strong opponents apart.

19 A brother wronged(S) is more unyielding than a fortified city;
    disputes are like the barred gates of a citadel.

20 From the fruit of their mouth a person’s stomach is filled;
    with the harvest of their lips they are satisfied.(T)

21 The tongue has the power of life and death,(U)
    and those who love it will eat its fruit.(V)

22 He who finds a wife finds what is good(W)
    and receives favor from the Lord.(X)

23 The poor plead for mercy,
    but the rich answer harshly.

24 One who has unreliable friends soon comes to ruin,
    but there is a friend who sticks closer than a brother.(Y)