Miyambo 18
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
18 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha;
iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu,
koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera.
Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya,
kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu;
kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano;
pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake,
ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma;
amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake
ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba;
wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba;
chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada,
koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani,
umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda,
koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina;
amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira
yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye
mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano;
amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba,
koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake.
Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.
Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino
ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Munthu wosauka amapempha
koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso,
koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
Proverbs 18
New International Version
18 An unfriendly person pursues selfish ends
and against all sound judgment starts quarrels.
2 Fools find no pleasure in understanding
but delight in airing their own opinions.(A)
3 When wickedness comes, so does contempt,
and with shame comes reproach.
4 The words of the mouth are deep waters,(B)
but the fountain of wisdom is a rushing stream.
6 The lips of fools bring them strife,
and their mouths invite a beating.(E)
8 The words of a gossip are like choice morsels;
they go down to the inmost parts.(H)
9 One who is slack in his work
is brother to one who destroys.(I)
11 The wealth of the rich is their fortified city;(L)
they imagine it a wall too high to scale.
12 Before a downfall the heart is haughty,
but humility comes before honor.(M)
13 To answer before listening—
that is folly and shame.(N)
14 The human spirit can endure in sickness,
but a crushed spirit who can bear?(O)
15 The heart of the discerning acquires knowledge,(P)
for the ears of the wise seek it out.
16 A gift(Q) opens the way
and ushers the giver into the presence of the great.
17 In a lawsuit the first to speak seems right,
until someone comes forward and cross-examines.
18 Casting the lot settles disputes(R)
and keeps strong opponents apart.
19 A brother wronged(S) is more unyielding than a fortified city;
disputes are like the barred gates of a citadel.
20 From the fruit of their mouth a person’s stomach is filled;
with the harvest of their lips they are satisfied.(T)
23 The poor plead for mercy,
but the rich answer harshly.
24 One who has unreliable friends soon comes to ruin,
but there is a friend who sticks closer than a brother.(Y)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.