Add parallel Print Page Options

Mlandu wa Yehova ndi Israeli

Tamverani zimene Yehova akunena:

“Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri;
    zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri;
    tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi.
Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake;
    Iye akutsutsa Aisraeli.

“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani?
    Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto
    ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo.
Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni,
    pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Anthu anga, kumbukirani
    zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani
    ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha.
Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala,
    kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”

Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova
    ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba?
Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza,
    ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000,
    kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta?
Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga?
    Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino.
    Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe?
Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo
    ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Kulakwa kwa Israeli ndi Chilango chake

Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda
    ndi nzeru kuopa dzina lanu.
    “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala
    chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo,
    ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo,
    ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa;
    anthu ake ndi abodza
    ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani,
    kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta;
    mudzakhalabe ndi njala.
Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika,
    chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola.
    Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito.
    Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri
    ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu,
    ndi khalidwe lawo lonse.
Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe
    ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu;
    mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

The Lord’s Case Against Israel

Listen to what the Lord says:

“Stand up, plead my case before the mountains;(A)
    let the hills hear what you have to say.

“Hear,(B) you mountains, the Lord’s accusation;(C)
    listen, you everlasting foundations of the earth.
For the Lord has a case(D) against his people;
    he is lodging a charge(E) against Israel.

“My people, what have I done to you?
    How have I burdened(F) you?(G) Answer me.
I brought you up out of Egypt(H)
    and redeemed you from the land of slavery.(I)
I sent Moses(J) to lead you,
    also Aaron(K) and Miriam.(L)
My people, remember
    what Balak(M) king of Moab plotted
    and what Balaam son of Beor answered.
Remember your journey from Shittim(N) to Gilgal,(O)
    that you may know the righteous acts(P) of the Lord.”

With what shall I come before(Q) the Lord
    and bow down before the exalted God?
Shall I come before him with burnt offerings,
    with calves a year old?(R)
Will the Lord be pleased with thousands of rams,(S)
    with ten thousand rivers of olive oil?(T)
Shall I offer my firstborn(U) for my transgression,
    the fruit of my body for the sin of my soul?(V)
He has shown you, O mortal, what is good.
    And what does the Lord require of you?
To act justly(W) and to love mercy
    and to walk humbly[a](X) with your God.(Y)

Israel’s Guilt and Punishment

Listen! The Lord is calling to the city—
    and to fear your name is wisdom—
    “Heed the rod(Z) and the One who appointed it.[b]
10 Am I still to forget your ill-gotten treasures, you wicked house,
    and the short ephah,[c] which is accursed?(AA)
11 Shall I acquit someone with dishonest scales,(AB)
    with a bag of false weights?(AC)
12 Your rich people are violent;(AD)
    your inhabitants are liars(AE)
    and their tongues speak deceitfully.(AF)
13 Therefore, I have begun to destroy(AG) you,
    to ruin[d] you because of your sins.
14 You will eat but not be satisfied;(AH)
    your stomach will still be empty.[e]
You will store up but save nothing,(AI)
    because what you save[f] I will give to the sword.
15 You will plant but not harvest;(AJ)
    you will press olives but not use the oil,
    you will crush grapes but not drink the wine.(AK)
16 You have observed the statutes of Omri(AL)
    and all the practices of Ahab’s(AM) house;
    you have followed their traditions.(AN)
Therefore I will give you over to ruin(AO)
    and your people to derision;
    you will bear the scorn(AP) of the nations.[g]

Footnotes

  1. Micah 6:8 Or prudently
  2. Micah 6:9 The meaning of the Hebrew for this line is uncertain.
  3. Micah 6:10 An ephah was a dry measure.
  4. Micah 6:13 Or Therefore, I will make you ill and destroy you; / I will ruin
  5. Micah 6:14 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  6. Micah 6:14 Or You will press toward birth but not give birth, / and what you bring to birth
  7. Micah 6:16 Septuagint; Hebrew scorn due my people