Add parallel Print Page Options

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

92 Nʼkwabwino kutamanda Yehova
    ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
Kulengeza chikondi chanu mmawa,
    ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi
    ndi mayimbidwe abwino a zeze.

Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;
    Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,
    maganizo anu ndi ozamadi!
Munthu wopanda nzeru sadziwa,
    zitsiru sizizindikira,
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu
    ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,
adzawonongedwa kwamuyaya.

Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

Zoonadi adani anu Yehova,
    zoonadi adani anu adzawonongeka;
    onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;
    mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,
    makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,
    adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,
    adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,
    adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;
    Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

Psalm 92[a]

A psalm. A song. For the Sabbath day.

It is good to praise the Lord
    and make music(A) to your name,(B) O Most High,(C)
proclaiming your love in the morning(D)
    and your faithfulness at night,
to the music of the ten-stringed lyre(E)
    and the melody of the harp.(F)

For you make me glad by your deeds, Lord;
    I sing for joy(G) at what your hands have done.(H)
How great are your works,(I) Lord,
    how profound your thoughts!(J)
Senseless people(K) do not know,
    fools do not understand,
that though the wicked spring up like grass
    and all evildoers flourish,
    they will be destroyed forever.(L)

But you, Lord, are forever exalted.

For surely your enemies(M), Lord,
    surely your enemies will perish;
    all evildoers will be scattered.(N)
10 You have exalted my horn[b](O) like that of a wild ox;(P)
    fine oils(Q) have been poured on me.
11 My eyes have seen the defeat of my adversaries;
    my ears have heard the rout of my wicked foes.(R)

12 The righteous will flourish(S) like a palm tree,
    they will grow like a cedar of Lebanon;(T)
13 planted in the house of the Lord,
    they will flourish in the courts of our God.(U)
14 They will still bear fruit(V) in old age,
    they will stay fresh and green,
15 proclaiming, “The Lord is upright;
    he is my Rock, and there is no wickedness in him.(W)

Footnotes

  1. Psalm 92:1 In Hebrew texts 92:1-15 is numbered 92:2-16.
  2. Psalm 92:10 Horn here symbolizes strength.