Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo.

66 Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
    Imbani ulemerero wa dzina lake;
    kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu!
    Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri
    kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Dziko lonse lapansi limaweramira inu;
    limayimba matamando kwa Inu;
    limayimba matamando pa dzina lanu.”
            Sela.

Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita,
    ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma,
    iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi.
    Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya,
    maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina.
    Anthu owukira asadzitukumule.

Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu,
    mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Iye watchinjiriza miyoyo yathu
    ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa;
    munatiyenga ngati siliva.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende
    ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu;
    ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi,
    koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.

13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza
    ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza
    ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu
    ndi chopereka cha nkhosa zazimuna;
    ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi.
            Sela

16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu.
    Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga,
    matamando ake anali pa lilime panga.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga
    Ambuye sakanamvera;
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera
    ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Matamando akhale kwa Mulungu
    amene sanakane pemphero langa
    kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

Psalm 66

For the director of music. A song. A psalm.

Shout for joy to God, all the earth!(A)
    Sing the glory of his name;(B)
    make his praise glorious.(C)
Say to God, “How awesome are your deeds!(D)
    So great is your power
    that your enemies cringe(E) before you.
All the earth bows down(F) to you;
    they sing praise(G) to you,
    they sing the praises of your name.”[a]

Come and see what God has done,
    his awesome deeds(H) for mankind!
He turned the sea into dry land,(I)
    they passed through(J) the waters on foot—
    come, let us rejoice(K) in him.
He rules forever(L) by his power,
    his eyes watch(M) the nations—
    let not the rebellious(N) rise up against him.

Praise(O) our God, all peoples,
    let the sound of his praise be heard;
he has preserved our lives(P)
    and kept our feet from slipping.(Q)
10 For you, God, tested(R) us;
    you refined us like silver.(S)
11 You brought us into prison(T)
    and laid burdens(U) on our backs.
12 You let people ride over our heads;(V)
    we went through fire and water,
    but you brought us to a place of abundance.(W)

13 I will come to your temple with burnt offerings(X)
    and fulfill my vows(Y) to you—
14 vows my lips promised and my mouth spoke
    when I was in trouble.
15 I will sacrifice fat animals to you
    and an offering of rams;
    I will offer bulls and goats.(Z)

16 Come and hear,(AA) all you who fear God;
    let me tell(AB) you what he has done for me.
17 I cried out to him with my mouth;
    his praise was on my tongue.
18 If I had cherished sin in my heart,
    the Lord would not have listened;(AC)
19 but God has surely listened
    and has heard(AD) my prayer.
20 Praise be to God,
    who has not rejected(AE) my prayer
    or withheld his love from me!

Footnotes

  1. Psalm 66:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 7 and 15.