Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.

65 Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;
    kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
Inu amene mumamva pemphero,
    kwa inu anthu onse adzafika.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,
    Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
Odala iwo amene inu muwasankha
    ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!
Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,
    za mʼNyumba yanu yoyera.

Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,
    Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi
    ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,
    mutadziveka nokha ndi mphamvu.
Amene munakhalitsa bata nyanja
    kukokoma kwa mafunde ake,
    ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;
    kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.
    Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.

Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;
    Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi
    kuti upereke tirigu kwa anthu,
    pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,
    mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,
    ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;
    mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta
    ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;
    izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

Psalm 65[a]

For the director of music. A psalm of David. A song.

Praise awaits[b] you, our God, in Zion;(A)
    to you our vows will be fulfilled.(B)
You who answer prayer,
    to you all people will come.(C)
When we were overwhelmed by sins,(D)
    you forgave[c] our transgressions.(E)
Blessed are those you choose(F)
    and bring near(G) to live in your courts!
We are filled with the good things of your house,(H)
    of your holy temple.

You answer us with awesome and righteous deeds,(I)
    God our Savior,(J)
the hope of all the ends of the earth(K)
    and of the farthest seas,(L)
who formed the mountains(M) by your power,
    having armed yourself with strength,(N)
who stilled the roaring of the seas,(O)
    the roaring of their waves,
    and the turmoil of the nations.(P)
The whole earth is filled with awe at your wonders;
    where morning dawns, where evening fades,
    you call forth songs of joy.(Q)

You care for the land and water it;(R)
    you enrich it abundantly.(S)
The streams of God are filled with water
    to provide the people with grain,(T)
    for so you have ordained it.[d]
10 You drench its furrows and level its ridges;
    you soften it with showers(U) and bless its crops.
11 You crown the year with your bounty,(V)
    and your carts overflow with abundance.(W)
12 The grasslands of the wilderness overflow;(X)
    the hills are clothed with gladness.(Y)
13 The meadows are covered with flocks(Z)
    and the valleys are mantled with grain;(AA)
    they shout for joy and sing.(AB)

Footnotes

  1. Psalm 65:1 In Hebrew texts 65:1-13 is numbered 65:2-14.
  2. Psalm 65:1 Or befits; the meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  3. Psalm 65:3 Or made atonement for
  4. Psalm 65:9 Or for that is how you prepare the land