Masalimo 64
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
64 Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
amayankhula zobisa misampha yawo;
ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
ndi kuwasandutsa bwinja;
onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 Anthu onse adzachita mantha;
adzalengeza ntchito za Mulungu
ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
ndi kubisala mwa Iye,
owongoka mtima onse atamande Iye!
Psalm 64
New International Version
Psalm 64[a]
For the director of music. A psalm of David.
2 Hide me from the conspiracy(C) of the wicked,(D)
from the plots of evildoers.
3 They sharpen their tongues like swords(E)
and aim cruel words like deadly arrows.(F)
4 They shoot from ambush at the innocent;(G)
they shoot suddenly, without fear.(H)
5 They encourage each other in evil plans,
they talk about hiding their snares;(I)
they say, “Who will see it[b]?”(J)
6 They plot injustice and say,
“We have devised a perfect plan!”
Surely the human mind and heart are cunning.
Footnotes
- Psalm 64:1 In Hebrew texts 64:1-10 is numbered 64:2-11.
- Psalm 64:5 Or us
Psalm 64
King James Version
64 Hear my voice, O God, in my prayer: preserve my life from fear of the enemy.
2 Hide me from the secret counsel of the wicked; from the insurrection of the workers of iniquity:
3 Who whet their tongue like a sword, and bend their bows to shoot their arrows, even bitter words:
4 That they may shoot in secret at the perfect: suddenly do they shoot at him, and fear not.
5 They encourage themselves in an evil matter: they commune of laying snares privily; they say, Who shall see them?
6 They search out iniquities; they accomplish a diligent search: both the inward thought of every one of them, and the heart, is deep.
7 But God shall shoot at them with an arrow; suddenly shall they be wounded.
8 So they shall make their own tongue to fall upon themselves: all that see them shall flee away.
9 And all men shall fear, and shall declare the work of God; for they shall wisely consider of his doing.
10 The righteous shall be glad in the Lord, and shall trust in him; and all the upright in heart shall glory.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.