Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

64 Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
    tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
    ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
    amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
    amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
    amayankhula zobisa misampha yawo;
    ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
    “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
    Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
    mwadzidzidzi adzakanthidwa.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
    ndi kuwasandutsa bwinja;
    onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

Anthu onse adzachita mantha;
    adzalengeza ntchito za Mulungu
    ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
    ndi kubisala mwa Iye,
    owongoka mtima onse atamande Iye!

Psalm 64[a]

For the director of music. A psalm of David.

Hear me, my God, as I voice my complaint;(A)
    protect my life from the threat of the enemy.(B)

Hide me from the conspiracy(C) of the wicked,(D)
    from the plots of evildoers.
They sharpen their tongues like swords(E)
    and aim cruel words like deadly arrows.(F)
They shoot from ambush at the innocent;(G)
    they shoot suddenly, without fear.(H)

They encourage each other in evil plans,
    they talk about hiding their snares;(I)
    they say, “Who will see it[b]?”(J)
They plot injustice and say,
    “We have devised a perfect plan!”
    Surely the human mind and heart are cunning.

But God will shoot them with his arrows;
    they will suddenly be struck down.
He will turn their own tongues against them(K)
    and bring them to ruin;
    all who see them will shake their heads(L) in scorn.(M)
All people will fear;(N)
    they will proclaim the works of God
    and ponder what he has done.(O)

10 The righteous will rejoice in the Lord(P)
    and take refuge in him;(Q)
    all the upright in heart will glory in him!(R)

Footnotes

  1. Psalm 64:1 In Hebrew texts 64:1-10 is numbered 64:2-11.
  2. Psalm 64:5 Or us