Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

63 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,
    moona mtima ine ndimakufunafunani;
moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,
    thupi langa likulakalaka inu,
mʼdziko lowuma ndi lotopetsa
    kumene kulibe madzi.

Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika
    ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Chifukwa chikondi chanu
    ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,
    ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.
    Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

Pa bedi panga ndimakumbukira inu;
    ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Chifukwa ndinu thandizo langa,
    ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Moyo wanga umakangamira Inu;
    dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;
    adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga
    ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;
    onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,
    koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Psalm 63[a]

A psalm of David. When he was in the Desert of Judah.

You, God, are my God,
    earnestly I seek you;
I thirst for you,(A)
    my whole being longs for you,
in a dry and parched land
    where there is no water.(B)

I have seen you in the sanctuary(C)
    and beheld your power and your glory.(D)
Because your love is better than life,(E)
    my lips will glorify you.
I will praise you as long as I live,(F)
    and in your name I will lift up my hands.(G)
I will be fully satisfied as with the richest of foods;(H)
    with singing lips my mouth will praise you.

On my bed I remember you;
    I think of you through the watches of the night.(I)
Because you are my help,(J)
    I sing in the shadow of your wings.(K)
I cling to you;(L)
    your right hand upholds me.(M)

Those who want to kill me will be destroyed;(N)
    they will go down to the depths of the earth.(O)
10 They will be given over to the sword(P)
    and become food for jackals.(Q)

11 But the king will rejoice in God;
    all who swear by God will glory in him,(R)
    while the mouths of liars will be silenced.(S)

Footnotes

  1. Psalm 63:1 In Hebrew texts 63:1-11 is numbered 63:2-12.