Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

62 Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;
    chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
    Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?
    Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,
    ngati mpanda wogwedezeka?
Iwo akufunitsitsa kumugwetsa
    kuti achoke pa malo ake apamwamba.
    Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.
Ndi pakamwa pawo amadalitsa
    koma mʼmitima yawo amatemberera.

Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;
    chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
    Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:
    Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;
    khuthulani mitima yanu kwa Iye,
    pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.
            Sela

Anthu wamba ndi mpweya chabe;
    anthu apamwamba ndi bodza chabe;
ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;
    iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
10 Musadalire kulanda mwachinyengo
    kapena katundu wobedwa;
ngakhale chuma chanu chichuluke,
    musayike mtima wanu pa icho.

11 Mulungu wayankhula kamodzi,
    ine ndamvapo zinthu ziwiri;
choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
12     komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.
Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu
    molingana ndi ntchito zake.

Psalm 62[a]

For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.

Truly my soul finds rest(A) in God;(B)
    my salvation comes from him.
Truly he is my rock(C) and my salvation;(D)
    he is my fortress,(E) I will never be shaken.(F)

How long will you assault me?
    Would all of you throw me down—
    this leaning wall,(G) this tottering fence?
Surely they intend to topple me
    from my lofty place;
    they take delight in lies.
With their mouths they bless,
    but in their hearts they curse.[b](H)

Yes, my soul, find rest in God;(I)
    my hope comes from him.
Truly he is my rock and my salvation;
    he is my fortress, I will not be shaken.
My salvation and my honor depend on God[c];
    he is my mighty rock, my refuge.(J)
Trust in him at all times, you people;(K)
    pour out your hearts to him,(L)
    for God is our refuge.

Surely the lowborn(M) are but a breath,(N)
    the highborn are but a lie.
If weighed on a balance,(O) they are nothing;
    together they are only a breath.
10 Do not trust in extortion(P)
    or put vain hope in stolen goods;(Q)
though your riches increase,
    do not set your heart on them.(R)

11 One thing God has spoken,
    two things I have heard:
“Power belongs to you, God,(S)
12     and with you, Lord, is unfailing love”;(T)
and, “You reward everyone
    according to what they have done.”(U)

Footnotes

  1. Psalm 62:1 In Hebrew texts 62:1-12 is numbered 62:2-13.
  2. Psalm 62:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 8.
  3. Psalm 62:7 Or / God Most High is my salvation and my honor