Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

60 Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.
    Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,
    konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;
    inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera
    kuti tisonkhanireko pothawa uta.

Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,
    kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
    “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu
    ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
    Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
    Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Mowabu ndi mbale yanga yosambira,
    pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,
    pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?
    Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife
    ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,
    pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano
    ndipo tidzapondaponda adani athu.

Psalm 60[a](A)

For the director of music. To the tune of “The Lily of the Covenant.” A miktam[b] of David. For teaching. When he fought Aram Naharaim[c] and Aram Zobah,[d] and when Joab returned and struck down twelve thousand Edomites in the Valley of Salt.(B)

You have rejected us,(C) God, and burst upon us;
    you have been angry(D)—now restore us!(E)
You have shaken the land(F) and torn it open;
    mend its fractures,(G) for it is quaking.
You have shown your people desperate times;(H)
    you have given us wine that makes us stagger.(I)
But for those who fear you, you have raised a banner(J)
    to be unfurled against the bow.[e]

Save us and help us with your right hand,(K)
    that those you love(L) may be delivered.
God has spoken from his sanctuary:
    “In triumph I will parcel out Shechem(M)
    and measure off the Valley of Sukkoth.(N)
Gilead(O) is mine, and Manasseh is mine;
    Ephraim(P) is my helmet,
    Judah(Q) is my scepter.(R)
Moab is my washbasin,
    on Edom I toss my sandal;
    over Philistia I shout in triumph.(S)

Who will bring me to the fortified city?
    Who will lead me to Edom?
10 Is it not you, God, you who have now rejected us
    and no longer go out with our armies?(T)
11 Give us aid against the enemy,
    for human help is worthless.(U)
12 With God we will gain the victory,
    and he will trample down our enemies.(V)

Footnotes

  1. Psalm 60:1 In Hebrew texts 60:1-12 is numbered 60:3-14.
  2. Psalm 60:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 60:1 Title: That is, Arameans of Northwest Mesopotamia
  4. Psalm 60:1 Title: That is, Arameans of central Syria
  5. Psalm 60:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.