Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

58 Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?
    Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,
    ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;
    kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,
    ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga,
    ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,
    Yehova khadzulani mano a mikango!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda
    pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;
    ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,
    kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,
    pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ndipo anthu adzanena kuti,
    “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;
    zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Psalm 58[a]

For the director of music. To the tune of “Do Not Destroy.” Of David. A miktam.[b]

Do you rulers indeed speak justly?(A)
    Do you judge people with equity?
No, in your heart you devise injustice,(B)
    and your hands mete out violence on the earth.(C)

Even from birth the wicked go astray;
    from the womb they are wayward, spreading lies.
Their venom is like the venom of a snake,(D)
    like that of a cobra that has stopped its ears,
that will not heed(E) the tune of the charmer,(F)
    however skillful the enchanter may be.

Break the teeth in their mouths, O God;(G)
    Lord, tear out the fangs of those lions!(H)
Let them vanish like water that flows away;(I)
    when they draw the bow, let their arrows fall short.(J)
May they be like a slug that melts away as it moves along,(K)
    like a stillborn child(L) that never sees the sun.

Before your pots can feel the heat of the thorns(M)
    whether they be green or dry—the wicked will be swept away.[c](N)
10 The righteous will be glad(O) when they are avenged,(P)
    when they dip their feet in the blood of the wicked.(Q)
11 Then people will say,
    “Surely the righteous still are rewarded;(R)
    surely there is a God who judges the earth.”(S)

Footnotes

  1. Psalm 58:1 In Hebrew texts 58:1-11 is numbered 58:2-12.
  2. Psalm 58:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 58:9 The meaning of the Hebrew for this verse is uncertain.