Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

55 Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,
    musakufulatire kupempha kwanga,
    mverani ndipo mundiyankhe.
Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
    chifukwa cha mawu a adani anga,
    chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;
pakuti andidzetsera masautso
    ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;
    mantha a imfa andigwera.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;
    mantha aakulu andithetsa nzeru.
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!
    Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
Ndikanathawira kutali
    ndi kukakhala mʼchipululu.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;
    kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;
    pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;
    nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;
    kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine
    ndikanapirira;
akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,
    ndikanakabisala.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,
    bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala
    pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;
    alowe mʼmanda ali amoyo
    pakuti choyipa chili pakati pawo.

16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,
    ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Madzulo, mmawa ndi masana
    ndimalira mowawidwa mtima,
    ndipo Iye amamva mawu anga.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa
    pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,
    ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,
    adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,
chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa
    ndipo saopa Mulungu.

20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;
    iye akuphwanya pangano ake.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala
    komabe nkhondo ili mu mtima mwake;
mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,
    komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.

22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova
    ndipo Iye adzakulimbitsani;
    Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa
    kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;
anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo
    sadzakhala moyo theka la masiku awo,

koma ine ndimadalira Inu.

Psalm 55[a]

For the director of music. With stringed instruments. A maskil[b] of David.

Listen to my prayer, O God,
    do not ignore my plea;(A)
    hear me and answer me.(B)
My thoughts trouble me and I am distraught(C)
    because of what my enemy is saying,
    because of the threats of the wicked;
for they bring down suffering on me(D)
    and assail(E) me in their anger.(F)

My heart is in anguish(G) within me;
    the terrors(H) of death have fallen on me.
Fear and trembling(I) have beset me;
    horror(J) has overwhelmed me.
I said, “Oh, that I had the wings of a dove!
    I would fly away and be at rest.
I would flee far away
    and stay in the desert;[c](K)
I would hurry to my place of shelter,(L)
    far from the tempest and storm.(M)

Lord, confuse the wicked, confound their words,(N)
    for I see violence and strife(O) in the city.(P)
10 Day and night they prowl(Q) about on its walls;
    malice and abuse are within it.
11 Destructive forces(R) are at work in the city;
    threats and lies(S) never leave its streets.

12 If an enemy were insulting me,
    I could endure it;
if a foe were rising against me,
    I could hide.
13 But it is you, a man like myself,
    my companion, my close friend,(T)
14 with whom I once enjoyed sweet fellowship(U)
    at the house of God,(V)
as we walked about
    among the worshipers.

15 Let death take my enemies by surprise;(W)
    let them go down alive to the realm of the dead,(X)
    for evil finds lodging among them.

16 As for me, I call to God,
    and the Lord saves me.
17 Evening,(Y) morning(Z) and noon(AA)
    I cry out in distress,
    and he hears my voice.
18 He rescues me unharmed
    from the battle waged against me,
    even though many oppose me.
19 God, who is enthroned from of old,(AB)
    who does not change—
he will hear(AC) them and humble them,
    because they have no fear of God.(AD)

20 My companion attacks his friends;(AE)
    he violates his covenant.(AF)
21 His talk is smooth as butter,(AG)
    yet war is in his heart;
his words are more soothing than oil,(AH)
    yet they are drawn swords.(AI)

22 Cast your cares on the Lord
    and he will sustain you;(AJ)
he will never let
    the righteous be shaken.(AK)
23 But you, God, will bring down the wicked
    into the pit(AL) of decay;
the bloodthirsty and deceitful(AM)
    will not live out half their days.(AN)

But as for me, I trust in you.(AO)

Footnotes

  1. Psalm 55:1 In Hebrew texts 55:1-23 is numbered 55:2-24.
  2. Psalm 55:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 55:7 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and in the middle of verse 19.