Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

53 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
    “Kulibe Mulungu.”
Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;
    palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano
    pa ana a anthu
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
    wofunafuna Mulungu.
Aliyense wabwerera,
    iwo onse pamodzi akhala oyipa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,
    ngakhale mmodzi.

Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;
    anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,
    ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu
    pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.
Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;
    inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!
    Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,
    lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

Psalm 53[a](A)

For the director of music. According to mahalath.[b] A maskil[c] of David.

The fool(B) says in his heart,
    “There is no God.”(C)
They are corrupt, and their ways are vile;
    there is no one who does good.

God looks down from heaven(D)
    on all mankind
to see if there are any who understand,(E)
    any who seek God.(F)
Everyone has turned away, all have become corrupt;
    there is no one who does good,
    not even one.(G)

Do all these evildoers know nothing?

They devour my people as though eating bread;
    they never call on God.
But there they are, overwhelmed with dread,
    where there was nothing to dread.(H)
God scattered the bones(I) of those who attacked you;(J)
    you put them to shame,(K) for God despised them.(L)

Oh, that salvation for Israel would come out of Zion!
    When God restores his people,
    let Jacob rejoice and Israel be glad!

Footnotes

  1. Psalm 53:1 In Hebrew texts 53:1-6 is numbered 53:2-7.
  2. Psalm 53:1 Title: Probably a musical term
  3. Psalm 53:1 Title: Probably a literary or musical term