Masalimo 53
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.
53 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano
pa ana a anthu
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
wofunafuna Mulungu.
3 Aliyense wabwerera,
iwo onse pamodzi akhala oyipa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,
ngakhale mmodzi.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;
anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,
ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu
pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.
Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;
inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!
Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,
lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Psalm 53
New International Version
Psalm 53[a](A)
For the director of music. According to mahalath.[b] A maskil[c] of David.
1 The fool(B) says in his heart,
“There is no God.”(C)
They are corrupt, and their ways are vile;
there is no one who does good.
2 God looks down from heaven(D)
on all mankind
to see if there are any who understand,(E)
any who seek God.(F)
3 Everyone has turned away, all have become corrupt;
there is no one who does good,
not even one.(G)
4 Do all these evildoers know nothing?
They devour my people as though eating bread;
they never call on God.
5 But there they are, overwhelmed with dread,
where there was nothing to dread.(H)
God scattered the bones(I) of those who attacked you;(J)
you put them to shame,(K) for God despised them.(L)
6 Oh, that salvation for Israel would come out of Zion!
When God restores his people,
let Jacob rejoice and Israel be glad!
Footnotes
- Psalm 53:1 In Hebrew texts 53:1-6 is numbered 53:2-7.
- Psalm 53:1 Title: Probably a musical term
- Psalm 53:1 Title: Probably a literary or musical term
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.