Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?
    Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,
    iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;
    lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,
    ntchito yako nʼkunyenga.
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.
    Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.
            Sela
Umakonda mawu onse opweteka,
    iwe lilime lachinyengo!

Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:
    iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;
    iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;
    adzamuseka nʼkumanena kuti,
“Pano tsopano pali munthu
    amene sanayese Mulungu linga lake,
koma anakhulupirira chuma chake chambiri
    nalimbika kuchita zoyipa!”

Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi
    wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu
    kwa nthawi za nthawi.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;
    chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera
    pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

Psalm 52[a]

For the director of music. A maskil[b] of David. When Doeg the Edomite(A) had gone to Saul and told him: “David has gone to the house of Ahimelek.”

Why do you boast of evil, you mighty hero?
    Why do you boast(B) all day long,(C)
    you who are a disgrace in the eyes of God?
You who practice deceit,(D)
    your tongue plots destruction;(E)
    it is like a sharpened razor.(F)
You love evil(G) rather than good,
    falsehood(H) rather than speaking the truth.[c]
You love every harmful word,
    you deceitful tongue!(I)

Surely God will bring you down to everlasting ruin:
    He will snatch you up and pluck(J) you from your tent;
    he will uproot(K) you from the land of the living.(L)
The righteous will see and fear;
    they will laugh(M) at you, saying,
“Here now is the man
    who did not make God his stronghold(N)
but trusted in his great wealth(O)
    and grew strong by destroying others!”

But I am like an olive tree(P)
    flourishing in the house of God;
I trust(Q) in God’s unfailing love
    for ever and ever.
For what you have done I will always praise you(R)
    in the presence of your faithful people.(S)
And I will hope in your name,(T)
    for your name is good.(U)

Footnotes

  1. Psalm 52:1 In Hebrew texts 52:1-9 is numbered 52:3-11.
  2. Psalm 52:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 52:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 5.