Masalimo 52
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”
52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?
Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,
iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
2 Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;
lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,
ntchito yako nʼkunyenga.
3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.
Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.
Sela
4 Umakonda mawu onse opweteka,
iwe lilime lachinyengo!
5 Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:
iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;
iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
6 Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;
adzamuseka nʼkumanena kuti,
7 “Pano tsopano pali munthu
amene sanayese Mulungu linga lake,
koma anakhulupirira chuma chake chambiri
nalimbika kuchita zoyipa!”
8 Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi
wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu
kwa nthawi za nthawi.
9 Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;
chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera
pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.
Psalm 52
New International Version
Psalm 52[a]
For the director of music. A maskil[b] of David. When Doeg the Edomite(A) had gone to Saul and told him: “David has gone to the house of Ahimelek.”
1 Why do you boast of evil, you mighty hero?
Why do you boast(B) all day long,(C)
you who are a disgrace in the eyes of God?
2 You who practice deceit,(D)
your tongue plots destruction;(E)
it is like a sharpened razor.(F)
3 You love evil(G) rather than good,
falsehood(H) rather than speaking the truth.[c]
4 You love every harmful word,
you deceitful tongue!(I)
5 Surely God will bring you down to everlasting ruin:
He will snatch you up and pluck(J) you from your tent;
he will uproot(K) you from the land of the living.(L)
6 The righteous will see and fear;
they will laugh(M) at you, saying,
7 “Here now is the man
who did not make God his stronghold(N)
but trusted in his great wealth(O)
and grew strong by destroying others!”
Footnotes
- Psalm 52:1 In Hebrew texts 52:1-9 is numbered 52:3-11.
- Psalm 52:1 Title: Probably a literary or musical term
- Psalm 52:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 5.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.