Masalimo 50
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Asafu.
50 Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,
akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi
kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri
Mulungu akuwala.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;
moto ukunyeketsa patsogolo pake,
ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga
ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,
amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,
pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,
iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;
ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,
kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako
kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga
ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri
ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani,
pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna
kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu,
kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso;
Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti,
“Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga
kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga
ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Ukaona wakuba umamutsatira,
umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa
ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako
ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete;
umaganiza kuti ndine wofanana nawe
koma ndidzakudzudzula
ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu
kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,
ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse
chipulumutso cha Mulungu.”
Psalm 50
New International Version
Psalm 50
A psalm of Asaph.
1 The Mighty One, God, the Lord,(A)
speaks and summons the earth
from the rising of the sun to where it sets.(B)
2 From Zion,(C) perfect in beauty,(D)
God shines forth.(E)
3 Our God comes(F)
and will not be silent;(G)
a fire devours(H) before him,(I)
and around him a tempest(J) rages.
4 He summons the heavens above,
and the earth,(K) that he may judge his people:(L)
5 “Gather to me this consecrated people,(M)
who made a covenant(N) with me by sacrifice.”
6 And the heavens proclaim(O) his righteousness,
for he is a God of justice.[a][b](P)
7 “Listen, my people, and I will speak;
I will testify(Q) against you, Israel:
I am God, your God.(R)
8 I bring no charges(S) against you concerning your sacrifices
or concerning your burnt offerings,(T) which are ever before me.
9 I have no need of a bull(U) from your stall
or of goats(V) from your pens,(W)
10 for every animal of the forest(X) is mine,
and the cattle on a thousand hills.(Y)
11 I know every bird(Z) in the mountains,
and the insects in the fields(AA) are mine.
12 If I were hungry I would not tell you,
for the world(AB) is mine, and all that is in it.(AC)
13 Do I eat the flesh of bulls
or drink the blood of goats?
14 “Sacrifice thank offerings(AD) to God,
fulfill your vows(AE) to the Most High,(AF)
15 and call(AG) on me in the day of trouble;(AH)
I will deliver(AI) you, and you will honor(AJ) me.”
16 But to the wicked person, God says:
“What right have you to recite my laws
or take my covenant(AK) on your lips?(AL)
17 You hate(AM) my instruction
and cast my words behind(AN) you.
18 When you see a thief, you join(AO) with him;
you throw in your lot with adulterers.(AP)
19 You use your mouth for evil
and harness your tongue to deceit.(AQ)
20 You sit and testify against your brother(AR)
and slander your own mother’s son.
21 When you did these things and I kept silent,(AS)
you thought I was exactly[c] like you.
But I now arraign(AT) you
and set my accusations(AU) before you.
Footnotes
- Psalm 50:6 With a different word division of the Hebrew; Masoretic Text for God himself is judge
- Psalm 50:6 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
- Psalm 50:21 Or thought the ‘I am’ was
- Psalm 50:23 Probable reading of the original Hebrew text; the meaning of the Masoretic Text for this phrase is uncertain.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.