Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.

Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,
    ganizirani za kusisima kwanga
Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,
    Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,
    pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;
    Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu
    ndi kudikira mwachiyembekezo.

Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;
    choyipa sichikhala pamaso panu.
Onyada sangathe kuyima pamaso panu;
    Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
Mumawononga iwo amene amanena mabodza;
    anthu akupha ndi achinyengo,
    Yehova amanyansidwa nawo.

Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,
    ndidzalowa mʼNyumba yanu;
mwa ulemu ndidzaweramira pansi
    kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu
    chifukwa cha adani anga ndipo
    wongolani njira yanu pamaso panga.

Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;
    mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.
Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;
    ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!
    Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.
Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,
    pakuti awukira Inu.

11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;
    lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.
Aphimbeni ndi chitetezo chanu,
    iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;
    mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

Psalm 5[a]

For the director of music. For pipes. A psalm of David.

Listen(A) to my words, Lord,
    consider my lament.(B)
Hear my cry for help,(C)
    my King and my God,(D)
    for to you I pray.

In the morning,(E) Lord, you hear my voice;
    in the morning I lay my requests before you
    and wait expectantly.(F)
For you are not a God who is pleased with wickedness;
    with you, evil people(G) are not welcome.
The arrogant(H) cannot stand(I)
    in your presence.
You hate(J) all who do wrong;
    you destroy those who tell lies.(K)
The bloodthirsty and deceitful
    you, Lord, detest.
But I, by your great love,
    can come into your house;
in reverence(L) I bow down(M)
    toward your holy temple.(N)

Lead me, Lord, in your righteousness(O)
    because of my enemies—
    make your way straight(P) before me.
Not a word from their mouth can be trusted;
    their heart is filled with malice.
Their throat is an open grave;(Q)
    with their tongues they tell lies.(R)
10 Declare them guilty, O God!
    Let their intrigues be their downfall.
Banish them for their many sins,(S)
    for they have rebelled(T) against you.
11 But let all who take refuge in you be glad;
    let them ever sing for joy.(U)
Spread your protection over them,
    that those who love your name(V) may rejoice in you.(W)

12 Surely, Lord, you bless the righteous;(X)
    you surround them(Y) with your favor as with a shield.(Z)

Footnotes

  1. Psalm 5:1 In Hebrew texts 5:1-12 is numbered 5:2-13.