Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

49 Imvani izi anthu a mitundu yonse;
    mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika,
    olemera pamodzinso ndi osauka:
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;
    mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo,
    ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika,
    pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Iwo amene adalira kulemera kwawo
    ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake
    kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali,
    palibe malipiro amene angakwanire,
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya
    ndi kusapita ku manda.

10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira;
    opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka
    ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya,
    malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo,
    ngakhale anatchula malo mayina awo.

12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani,
    adzafa ngati nyama.

13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha,
    ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula.
            Sela
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda,
    ndipo imfa idzawadya.
Olungama adzawalamulira mmawa;
    matupi awo adzavunda mʼmanda,
    kutali ndi nyumba zawo zaufumu.
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda;
    ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.

16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera,
    pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira,
    ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala,
    ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake,
    amene sadzaonanso kuwala.

20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru
    adzafa ngati nyama yakuthengo.

Psalm 49[a]

For the director of music. Of the Sons of Korah. A psalm.

Hear(A) this, all you peoples;(B)
    listen, all who live in this world,(C)
both low and high,(D)
    rich and poor alike:
My mouth will speak words of wisdom;(E)
    the meditation of my heart will give you understanding.(F)
I will turn my ear to a proverb;(G)
    with the harp(H) I will expound my riddle:(I)

Why should I fear(J) when evil days come,
    when wicked deceivers surround me—
those who trust in their wealth(K)
    and boast(L) of their great riches?(M)
No one can redeem the life of another
    or give to God a ransom for them—
the ransom(N) for a life is costly,
    no payment is ever enough—(O)
so that they should live on(P) forever
    and not see decay.(Q)
10 For all can see that the wise die,(R)
    that the foolish and the senseless(S) also perish,
    leaving their wealth(T) to others.(U)
11 Their tombs(V) will remain their houses[b] forever,
    their dwellings for endless generations,(W)
    though they had[c] named(X) lands after themselves.

12 People, despite their wealth, do not endure;(Y)
    they are like the beasts that perish.(Z)

13 This is the fate of those who trust in themselves,(AA)
    and of their followers, who approve their sayings.[d]
14 They are like sheep and are destined(AB) to die;(AC)
    death will be their shepherd
    (but the upright will prevail(AD) over them in the morning).
Their forms will decay in the grave,
    far from their princely mansions.
15 But God will redeem me from the realm of the dead;(AE)
    he will surely take me to himself.(AF)
16 Do not be overawed when others grow rich,
    when the splendor of their houses increases;
17 for they will take nothing(AG) with them when they die,
    their splendor will not descend with them.(AH)
18 Though while they live they count themselves blessed—(AI)
    and people praise you when you prosper—
19 they will join those who have gone before them,(AJ)
    who will never again see the light(AK) of life.

20 People who have wealth but lack understanding(AL)
    are like the beasts that perish.(AM)

Footnotes

  1. Psalm 49:1 In Hebrew texts 49:1-20 is numbered 49:2-21.
  2. Psalm 49:11 Septuagint and Syriac; Hebrew In their thoughts their houses will remain
  3. Psalm 49:11 Or generations, / for they have
  4. Psalm 49:13 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 15.